Search

Buchrezension

OH INDE! NDINALI OCHIMWA KOMA TSOPANO NDINE MWANA WA MULUNGU OPANDA UCHIMO POKHULUPILIRA MU UTHENGA WABWINO WA MADZI, MWAZI NDI MZIMU

  • Brenda Tembo
  • Zambia
  • 1212
  • 01/03/2024

English 1

HAVE YOU TRULY BEEN BORN AGAIN OF WATER AND THE SPIRIT? [New Revised Edition]

Rev. Paul C. Jong

  • ISBN9788928261482
  • Seiten369
  • Bewertung

OH INDE! NDINALI OCHIMWA KOMA TSOPANO NDINE MWANA WA MULUNGU OPANDA UCHIMO POKHULUPILIRA MU UTHENGA WABWINO WA MADZI, MWAZI NDI MZIMU
Ndikuthokoza Mulungu posindikiza buku lapadera lotchedwa KODI MWABADWADI MWATSOPANO MWA MADZI NDI MZIMU? Kudzera mwa mtumiki Wake REV PAUL C.JONG.
Kudzera mu kuwerenga buku limeneli, KODI MWABADWADI MWATSOPANO MWA MADZI NDI MZIMU? la REV PAUL C. JONG, ndamvetsetsa motheratu kuti ndinedi ndani monga munthu kupatula Yesu Kristu. Kuti ndinabadwa wa uchimo kwambiri, ndipo ndinaikidwira ku gahena zonse chifukwa cha machimo anga. Koma mathokozo akhale kwa Mwana Obadwa Yekha wa Mulungu, Yesu Kristu amene anadza ku dziko lino lapansi kusandulika m’thupi la munthu, ndipo pa zaka za 30 kupita ku Mtsinje wa Yordano kukakumana ndi Yohane Mbatizi amene anaimilira monga woimirira wa mtundu wa anthu komanso mkulu wa nsembe wotsiriza pa dziko lapansi pamene Iye anabatiza Yesu Kristu kuti apereke machimo anga onse otengera, akale, atsopano ndi a mtsogolo pa thupi la Yesu Kristu kudzera mu njira ya kuika kwa manja monga yodzodzedwa ndi Mulungu Atate M`chipangano Chakale mu (Levitiko 1:1-4, 16 ndime ya 21) yomwe imafanana ndi ubatizo wa Yesu kudzera mwa Yohane Mbatizi mu (Mateyu 3:13-17). Chifukwa chakuti tsopano ndimakhulupilira mu Choonadi chimenechi kuti Yesu Kristu anabatizidwa ndi Yohane Mbatizi kuti atenge machimo anga onse komanso machimo a aliyense padziko lapansi ndi kupita pa mtanda kuti alipire mphotho ya machimo anga, ndipo pa tsiku lachitatu kuukitsidwa kuti apereke moyo watsopano, ndakhala tsopano mwana wa Mulungu wopanda uchimo komanso olungama. Aleluya!! Ulemelero wonse ndi Ulemu ziperekedwe kwa Yesu Kristu.
Ndikupereka mathokozo anga kwa Mtumiki woona wa Mulungu, Rev. Paul C. Jong, pondidalitsa ine komanso dziko lonse lapansi ndi buku lapadera limeneli lokhala ndi mau enieni a chipulumutso omwe tsopano andipatsa ine mwayi wolowa Kumwamba monga ulendo wanga. Amen.

Brenda Tembo, Zambia.