• All e-books and audiobooks on The New Life Mission website are free
  • Explore multilingual sermons in global languages
  • Two new revised editions in English have been released
  • Check out our website translated into 27 languages
Search

Sermons

Mutu 4: Kuthetsa Machimo a Tsiku ndi Tsiku

[4-1] Uthenga Wabwino wa Chiombolo Chochuluka (Yohane 13:1-17)

Uthenga Wabwino wa Chiombolo Chochuluka (Yohane 13:1-17)
(Yohane 13:1-17)
“Koma pasanafike chikondwerero la Paska, Yesu, podziwa kuti nthawi yake idadza yakuchoka kutuluka m’dziko lino lapansi, kunka kwa Atate, m’mene anakonda ake a Iye yekha a m’dziko lapansi, anawakonda kufikira chimaliziro. Ndipo pokhala pamgonero, mdierekezi adatha kuika mu mtima wake wa Yudasi mwana wa Simoni Iskariote, kuti akampereke Iye, Yesu, podziwa kuti Atate adampatsa Iye zonse m’manja mwake, ndi kuti anachokera kwa Mulungu(God), namuka kwa Mulungu(God), ananyamuka pamgonero, navula malaya ake; ndipo m’mene adatenga chopukutira, anadzimanga m’chuuno. Pomwepo anathira madzi m’beseni, nayamba kusambitsa mapazi a ophunzira ake, ndi kuwapukuta ndi chopukutira, chimene anadzimanga nacho. Anadza pomwepo kwa Simoni Petro. Iyeyu ananena ndi Iye, Ambuye, kodi Inu mundisambitsa ine mapazi? Yesu anayankha nati kwa iye, Chimene ndichita Ine suchidziwa tsopano; koma udzadziwa m’tsogolo mwake. Petro ananena ndi Iye, Simudzasambitsa mapazi anga kunthawi yonse. Yesu anamyankha iye, Ngati sindikusambitsa iwe ulibe cholandira pamodzi ndi Ine. Simoni Petro ananena ndi Iye, Ambuye, si mapazi anga okha, komanso manja ndi mutu. Yesu ananena naye, Amene anatha kusamba alibe kusowa koma kusamba mapazi, koma ayera monse: ndipo inu ndinu oyera, koma si nonse ai. Pakuti anadziwa amene adzampereka Iye; chifukwa cha ichi anati, Simuli oyera nonse. Pamenepo, atatha Iye kusambitsa mapazi ao, ndi kutenga malaya ake, anaseamanso, nati kwa iwo, Nanga chimene ndakuchitirani inu, muchizindikira kodi? Inu munditcha Ine Mphunzitsi, ndi Ambuye: ndipo munena bwino; pakuti ndine amene. Chifukwa chake, ngati Ine Ambuye ndi Mphunzitsi, ndasambitsa mapazi anu, inunso muyenera kusambitsana mapazi wina ndi mnzake. Pakuti ndakupatsani inu chitsanzo, kuti, monga Ine ndakuchitirani inu, inunso muchite. Indetu, indetu, ndinena ndi inu, Kapolo sali wamkulu ndi mbuye wake; kapena mtumwi sali wamkulu ndi womtuma iye. Ngati mudziwa izi, odala inu ngati muzichita.”
 
 
Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu anasambitsa mapazi a Petro pasanafike tsiku la Paska? Posambitsa mapazi ake, Yesu ananena kuti, “Chimene ndichita Ine suchidziwa tsopano, koma udzadziwa m’tsogolo mwake.” Simoni Petro anali wophunzira wabwino koposa wa Yesu. Iye anakhulupilira kuti Yesu anali Mwana wa God ndipo anachitira umboni kuti Yesu anali Kristu. Ndipo pamene Yesu ankasambitsa mapazi ake, panali kwenikweni chifukwa chokwanira chochitira zimenezo. Pamene Petro anavomereza Chikhulupiriro chake kuti Yesu anali Kristu, zinatanthauza kuti iye anakhulupilira Yesu kukhala Mpulumutsi amene adzapulumutsa iye ku machimo ake onse.
 
Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu anasambitsa mapazi a ophunzira Iye asanapachikidwe?
Chifukwa chakuti Iye ankafuna kuti ophunzira Wake amvetsetse chipulumutso changwiro.
 
Kodi ndi chifukwa chiyani Iye anasambitsa mapazi a Petro? Yesu ankadziwa kuti Petro posachedwapa adzamukana Iye katatu komanso kuti iye adzachita machimo ambiri m’tsogolo.
Ngati, Yesu atakwera kumwamba, Petro akadakhala ndi tchimo lirilonse lotsalira mu mtima mwake, iye sakanathanso kugwirizana ndi Yesu. Koma Yesu amadziwa zofooka zonse za ophunzira Wake, ndipo Iye sanafune kuti machimo awo adze pakati pa Iye ndi ophunzira Wake. Choncho, Iye anafunika kuwaphunzitsa kuti machimo awo onse anali atasambitsidwa kale. Icho ndiye chifukwa chimene Iye anasambitsira mapazi a ophunzira Wake. Yesu, asanafe ndi kuwasiya iwo, anaonetsetsa kuti anamvetsetsa uthenga wabwino wa ubatizo Wake komanso kuti Iye anachotsa kwathunthu machimo awo onse a moyo wawo wonse.
Yohane mutu wa 13 umalankhula za chipulumutso changwiro chimene Yesu adakwaniritsa kwa ophunzira Wake. Posambitsa mapazi ao, Yesu anauza iwo za mzeru ya uthenga wabwino wa ubatizo Wake umene anthu onse angatsukire zolakwa zao zonse.
“Musanyengedwe ndi mdierekezi m’tsogolo. Ndachotsa machimo anu onse ndi ubatizo Wanga mu Mtsinje wa Yordano ndipo Ndidzatenga chiweruzo cha iwo pa Mtanda. Kenako Ndidzaukitsidwa kwa akufa ndi kukwaniritsa chipulumutso cha kubadwa mwatsopano cha inu nonse. Kuti ndikuphunzitseni inu kuti Ndatsuka kale machimo anu a m’tsogolo, kuti ndikuphunzitseni inu uthenga wabwino woyambirira wa kuchotsa machimo, Ndikusambitsa mapazi anu Ndisanapachikidwe. Ichi ndi chinsinsi cha uthenga wabwino wa kubadwa mwatsopano. Inu nonse muyenera kukhulupilira motero.”
Ife tonse tiyenera kumvetsetsa chifukwa chimene Yesu anasambitsira mapazi a ophunzira ndi kudziwa chifukwa chimene Iye ananenera kuti, “Chimene ndichita Ine suchidziwa tsopano, koma udzadziwa m’tsogolo mwake.” Pokhapo ndi pamene ife tingakhulupilire mu uthenga wabwino wa kubadwa mwatsopano ndi kubadwanso mwatsopano kwenikweni tokha.
 
 
Iye Ananena mu Yohane 13
 
Kodi zolakwa ndi chiyani?
Iwo ndi machimo amene ife timachita tsiku lililonse chifukwa chakuti ndife ofooka.
 
Asanafe pa Mtanda, Yesu anapanga phwando la Paska ndi ophunzira Wake ndipo anawatsimikizira za uthenga wabwino wa kutsuka machimo awo posambitsa mapazi awo ndi manja Wake omwe.
“Yesu, podziwa kuti Atate adampatsa Iye zonse m’manja mwake, ndi kuti anachokera kwa Mulungu(God), namuka kwa Mulungu(God), ananyamuka pamgonero, navula malaya ake; ndipo m’mene adatenga chopukutira, anadzimanga m’chuuno. Pomwepo anathira madzi m’beseni, nayamba kusambitsa mapazi a ophunzira ake, ndi kuwapukuta ndi chopukutira, chimene anadzimanga nacho. Anadza pomwepo kwa Simoni Petro. Iyeyu ananena ndi Iye, Ambuye, kodi Inu mundisambitsa ine mapazi? Yesu anayankha nati kwa iye, Chimene ndichita Ine suchidziwa tsopano; koma udzadziwa m’tsogolo mwake.” (Yohane 13:3-7)
Iye anaphunzitsa ophunzira Wake uthenga wabwino wa ubatizo ndi chitetezero cha machimo kudzera m’madzi a ubatizo Wake.
Pa nthawi imeneyo, pokhala wokhulupirika kwa Yesu, Petro sanatha kumvetsetsa chifukwa chimene Yesu anasambitsira mapazi ake. Atatha Yesu kulankhula naye, njira imene iye anakhulupirira mwa Yesu inasintha. Yesu ankafuna kumuphunzitsa za kutsuka machimo, za uthenga wabwino wa madzi a ubatizo Wake.
Iye anali ndi nkhawa kuti Petro mwina sadzatha kudza kwa Iye chifukwa cha machimo ake onse a m’tsogolo, makamaka machimo a thupi lake m’tsogolo. Yesu anasambitsa mapazi ao kuti mdierekezi asatenge Chikhulupiriro cha ophunzira Wake. Pambuyo pake, Petro anamvetsetsa chifukwa chake.
Yesu anakonza njira kuti aliyense amene wakhulupilira m’madzi a ubatizo Wake, ndi mwazi aomboledwe ku machimo ake kwamuyaya.
Mu Yohane mutu wa 13, mau amene Iye analankhula pamene ankasambitsa mapazi a ophunzira Wake analembedwa. Iwo ndi mau ofunika kwambiri amene obadwa mwatsopano okha ndi amene angamvetsetsedi.
Chifukwa chimene Yesu anasambitsira mapazi a ophunzira Ake pasanafike phwando la Paska kunali kuwathandiza iwo kuzindikira kuti Iye adatsuka kale machimo a moyo wao wonse. Yesu ananena kuti, “Chifukwa chimene Ndikutsukira mapazi anu simukudziwa tsopano, koma inu mudzachidziwa m’tsogolo mwake.” Mau amenewa kwa Petro anali ndi choonadi cha kubadwa mwatsopano.
Ife tonse tiyenera kudziwa ndi kukhulupilira mu Ubatizo wa Yesu, umene watsuka zolakwa zathu zonse. Ubatizo wa Yesu pa Yordano unali uthenga wabwino ‘wopatsira’ machimo onse, poika manja. Ife tonse tiyenera kukhulupilira m’mau a Yesu. Iye anachotsa machimo onse a dziko lapansi kudzera mu ubatizo Wake ndipo anafafaniza uchimo poweruzidwa ndi kupachikidwa. Yesu anabatizidwa kuti achotse machimo onse a anthu onse.
 
 

Kuchotsa Zolakwa Zonse za Moyo Wathu Wonse Kunakwaniritsidwa ndi Ubatizo ndi Mwazi wa Yesu

 
Kodi ‘msapha’ wa mdierekezi pa wolungama ndi chiyani?
Mdierekezi amayesa kunyenga olungama kuti awapangenso iwo kukhala ochimwa.
 
Yesu ankadziwa bwino kuti pamene Iye anapachikidwa, anaukitsidwa, ndi kukwera kumwamba, mdierekezi ndi ofalitsa Chikhulupiriro chabodza adzabwera ndi kuyesa kunyenga ophunzira. Ife tingaone ndi umboni wa Petro wakuti, “Inu ndinu Khristu, Mwana wa Mulungu(God) wamoyo.” kuti Iye anakhulupilira mwa Yesu. Komabe, Yesu ankafuna kukumbutsa Petro kachiwiri kuti asunge uthenga wabwino wa kutsuka machimo mu mtima. Uthenga wabwino umenewo unali Ubatizo wa Yesu, umene Iye anachotsera machimo onse a dziko lapansi. Iye ankafuna kuphunzitsa uwo kachiwiri kwa Petro ndi ophunzira komanso kwa ife, kwa iwo amene adzabwera m’tsogolo. “Chimene ndichita Ine suchidziwa tsopano, koma udzadziwa m’tsogolo mwake.”
Nthawi zonse pamene ophunzira a Yesu achimwa, mdierekezi amayesa ndi kutsutsa iwo, kunena kuti, “Ona! Ngati iwe ukuchitabe machimo, kodi iwe unganene bwanji kuti ndiwe opanda uchimo? Iwe sunapulumutsidwe. Ndiwe ochimwa chabe.” Kuti apewe zimenezo, Yesu anawauza iwo kuti Chikhulupiriro chao mu Ubatizo wa Yesu chidatsuka kale machimo a moyo wao wonse ― a kale, a tsopano, ndi a m’tsogolo. 
“Inu nonse mukudziwa kuti Ndinabatizidwa! Chifukwa chimene Ndinabatizidwira pa Yordano kunali kutsuka machimo a moyo wanu wonse, komanso uchimo woyambirira wa mtundu wa anthu. Kodi inu mukutha kumvetsetsa tsopano chifukwa chimene Ndinabatizidwira, chifukwa chimene Ndiyenera kupachikidwa ndi kufa pa Mtanda?” Yesu anasambitsa mapazi a ophunzira Wake kuti awaonetse kuti Iye adachotsa machimo awo onse a tsiku ndi tsiku kudzera mu ubatizo Wake ndipo kuti Iye adzatenga chiweruzo chawo pa Mtanda.
Tsopano, inu ndi ine taomboledwa ku machimo athu onse ndi Chikhulupiriro chathu mu uthenga wabwino wa Ubatizo wa Yesu ndi mwazi, zimene ndi kutsuka machimo athu onse. Yesu anabatizidwa ndi kupachikidwa chifukwa cha ife. Iye watsuka machimo athu onse ndi ubatizo Wake ndi mwazi. Aliyense amene amadziwa ndi kukhulupilira mu uthenga wabwino wa chitetezero cha machimo, aliyense amene amakhulupilira mu choonadi, ndi owomboledwa ku machimo ake onse.
Ndiye kodi munthu ayenera kuchita chiyani akapulumutsidwa? Iye ayenera kuvomereza machimo ake tsiku lililonse ndi kukhulupilira mu chipulumutso cha ubatizo ndi mwazi wa Yesu, uthenga wabwino wa chitetezero cha machimo onse. Munthu ayenera kutenga mu mtima mwake uthenga wabwino wakuti Yesu anachotsa machimo onse ndi ubatizo Wake ndi mwazi Wake.
Chifukwa chakuti inu mumachimwanso, kodi inu mudzakhalanso ochimwa? Ayi. Podziwa kuti Yesu anachotsa machimo athu onse, kodi ife tingakhalenso bwanji ochimwa? Ubatizo wa Yesu ndi mwazi Wake pa Mtanda zinali uthenga wabwino wa chitetezero cha machimo athu onse. Aliyense amene amakhulupilira mu uthenga wabwino woyambirira uwu wa kufafaniza machimo amabadwanso mwatsopano monga ‘munthu wolungama’.
 
 

Olungama Sangakhalenso konse Ochimwa

 
Kodi ndi chifukwa chiyani olungama sangakhalenso konse ochimwa?
Chifukwa chakuti Yesu anachotsa kale machimo a moyo wao wonse
 
Ngati inu mumakhulupilira mu uthenga wabwino wa kufafaniza machimo, wa madzi ndi Mzimu Woyera, koma kumvabe kuti ndinu ochimwa chifukwa cha zolakwa zanu tsiku ndi tsiku, ndiye inu muyenera kupita ku Yordano kumene Yesu anabatizidwa kuti atenge machimo anu onse. Ngati inu mwakhalanso ochimwa pambuyo pokutsukidwa machimo anu, kodi Yesu ayenera kubatizidwanso mobwereza? Inu muyenera kukhala ndi Chikhulupiriro mu kuchotsedwa kwa machimo anu mu uthenga wabwino wa ubatizo wa Yesu. Inu muyenera kukumbukira kuti Yesu anatenga machimo anu onse kamodzi kokha kudzera mu ubatizo Wake. Inu muyenera kukhala ndi Chikhulupiriro chosagwezeka mwa Yesu Kristu monga Mpulumutsi wanu. 
Kukhulupilira mwa Yesu monga Mpulumutsi wanu zikutanthauza kuti inu mumakhulupilira mu ubatizo wa Yesu, umene unachotsa machimo a moyo wanu wonse. Ngati inu kwenikweni mumakhulupilira mu ubatizo, Mtanda, imfa, ndi kuuka kwa Yesu, simungakhalenso ochimwa konse, ziribe kanthu kuti ndi tchimo lotani limene mwachita. Mwaomboledwa ku machimo onse a moyo wanu wonse kudzera mu Chikhulupiriro chanu.
Yesu Kristu anatsukanso machimo a m’tsogolo, ngakhale machimo amene ife timachita chifukwa cha zofooka zathu. Ndipo chifukwa chakuti Yesu ankayenera kutsindika kufunika kwa ubatizo Wake, Iye anasambitsa mapazi a ophunzira Ake ndi madzi kuti afanizire uthenga wabwino wa kuchotsa machimo, ndiye ubatizo. Yesu Kristu anabatizidwa, kupachikidwa, kuukitsidwa, ndi kukwera kumwamba kuti akwaniritse lonjezo la God la chitetezero chochuluka cha machimo onse a dziko lapansi ndi kupulumutsa anthu onse. Zotsatira zake, ophunzira Ake anatha kulalikira uthenga wabwino wa chitetezero cha machimo, Ubatizo wa Yesu, Mtanda ndi kuuka, kuyambira pamenepo mpaka mapeto a miyoyo yao.
 
 
Kufooka kwa Thupi la Petro
 
Kodi ndi chifukwa chiyani Petro anakana Yesu?
Chifukwa chakuti iye anali ofooka
 
Baibulo limatiuza ife kuti pamene Petro anakumana ndi antchito a Kayafa mkulu wa ansembe ndi kudzudzulidwa kuti anali m’modzi wa otsatira a Yesu, iye anakana kawiri, kunena kuti, “Sindidziwa Munthuyo!” Kenako iye anatembelera ndi kulumbira kachitatu.
Tiyeni tiwerenge ndimeyi apa. Kuchokera mu Mateyu 26:69, “Ndipo Petro adakhala pabwalo: ndipo mdzakazi anadza kwa iye, nanena, Iwenso unali ndi Yesu wa ku Galileya. Koma iye anakana pamaso pa anthu onse, kuti, Chimene unena sindichidziwa. Ndipo pamene iye anatuluka kunka kuchipata, mkazi wina anamuona, nati kwa iwo a pomwepo, Uyonso anali ndi Yesu Mnazarayo. Ndipo anakananso ndi chilumbiro, kuti, Sindidziwa munthuyo. Ndipo popita nthawi yaing’ono, iwo akuimapo anadza, nati kwa Petro, Zoonadi, iwenso uli wa iwo; pakuti malankhulidwe ako akuzindikiritsa iwe. Pamenepo iye anayamba kutemberera ndi kulumbira, kuti, Sindidziwa munthuyo. Ndipo pompo tambala analira. Ndipo Petro anakumbukira mau amene Yesu adati, Asanalire tambala udzandikana katatu. Ndipo anatulukira kunja, nalira ndi kuwawa mtima.” (Mateyu 26:69-75)
Petro kwenikweni anakhulupilira ndi kutsata Iye mokhulupirika. Iye ankakhulupirira kuti Yesu anali “Inu ndinu Khristu, Mwana wa Mulungu(God) wamoyo.” Koma pamene Yesu anatengedwa kupita ku bwalo la Kayafa, pamene kunakhala koopsa kukhala pamodzi ndi Yesu, iye anakana ndi kumutemberera Yesu.
Petro sanadziwe kuti iye adzakamuka Yesu. Koma Yesu akadziwa kuti iye adzamukana. Yesu ankadziwa kufooka kwa Petro bwino bwino. Choncho, Yesu anasambitsa mapazi a Petro ndi kumuphunzitsa iye uthenga wabwino wa chipulumutso monga kwalembedwa mu Yohane mutu wa 13 kuti, “Iwe udzachimwa m’tsogolo, koma ndatsuka kale machimo ako onse a m’tsogolo.”
Petro indedi anamkana Yesu pamene moyo wake unali pa chiswe, koma kunali kufooka kwa thupi lake kumene kunamupanga iye kuchita zimenezi. Choncho, kuti aphunzitse ophunzira Ake kuti Iye wapulumutsa iwo ku mphulupulu zao zonse za m’tsogolo, Yesu anasambitsiratu mapazi ao.
“Ndakupulumutsani kale inu ku machimo anu onse a m’tsogolonso. Ndipachikidwa chifukwa chakuti Ndinabatizidwa ndi kutenga machimo anu onse, ndipo ndidzalipira iwo onse kuti Ndikhale Mpulumutsi weniweni wa inu nonse. Ndine God wanu, Mpulumutsi wanu. Ndidzalipira kwathunthu machimo anu onse, ndipo ndidzakhala Mbusa wanu kudzera mu ubatizo Wanga ndi mwazi Wanga. Ndine Mbusa wa chipulumutso chanu.”
Kuti adzale choonadi ichi molimba m’mitima mwawo, Yesu anasambitsa mapazi awo phwando la Paska lisanafike. Ichi ndi choonadi cha uthenga wabwino.
Chifukwa chakuti thupi lathu ndi lofooka ngakhale pambuyo pobadwa mwatsopano, tidzachimwanso. Ndithudi, sitiyenera kuchimwa, koma monga momwe Petro anakumana ndi mavuto aakulu chifukwa cha tchimo losachita dala, ifenso tingachimwe popanda kwenikweni cholinga chochita choncho. Chifukwa chakuti timakhala mthupi, timatsogozedwa ku chionongeko ndi machimo athu. Thupi lidzachimwa malinga ngati tikukhala m’dziko lino lachikunja, koma Yesu anachotsa machimo onse amenewo ndi ubatizo Wake ndi mwazi Wake pa Mtanda.
Ife sitikana kuti Yesu ndi Mpulumutsi wathu, koma pamene ife tikukhala m’thupi, ife timapitiriza kuchitira machimo chifuniro cha God. Ndi chifukwa chakuti ndife obadwa a thupi.
Koma Yesu ankadziwa bwino kuti ndife ochimwa m’thupi. Yesu anakhala Mpulumutsi wathu polipira machimo athu onse ndi ubatizo Wake ndi mwazi. Iye watimasula ife ku machimo onse kudzera pokhulupilira mu chipulumutso Wake ndi kuuka Wake.
Mauthenga Abwino onse anayi amayamba ndi ubatizo wa Yesu kudzera mwa Yohane Mbatizi. Cholinga cha moyo Wake wa umunthu chinali kuti akwaniritse uthenga wabwino wa kubadwa mwatsopano, uthenga wabwino wa chipulumutso.
 
Kodi ife timachimwa motalika bwanji m’thupi?
Ife timachimwa miyoyo yathu yonse kufikira tsiku limene ife timafa.
 
Pamene Petro anamkana Iye osati kamodzi, kapena kawiri, koma katatu tambala asanalire, kodi izo zinaphwanya bwanji mtima wake? Kodi iye anamva bwanji manyazi? Iye analumbira pamaso pa Yesu kuti iye sadzampereka Iye. Iye anachimwa chifukwa cha kufooka kwa thupi lake, koma kodi anamva bwanji chisoni pamene anagonjera ku kufooka kwake ndi kukana Yesu osati kamodzi kokha, koma katatu? Kodi zinali zochititsa manyazi bwanji kwa iye pamene anayang’anso Yesu?
Koma Yesu ankadziwa zinthu zonse zimenezi ndi zina zambiri. Choncho, Iye ananena kuti, “Ndikudziwa kuti udzachimwanso. Koma Ndachotsa kale machimo onse amenewo ndi ubatizo Wanga, kuwopa kuti machimo ako angakugwetse ndi kukubwezanso kukhala wochimwa, ndiponso kuwopa kuti ungapeze kuti n’zosatheka kubwerera kwa Ine. Ndakhala Mpulumutsi wathunthu kwa iwe pobatizidwa ndi kuweruzidwa chifukwa cha machimo onse. Ndakhala God wako, Mbusa wako. Khulupilira mu uthenga wabwino wa kutsuka machimo ako. Ndidzapitiriza kukukonda ngakhale utachita machimo a thupi. Ndatsuka kale mphulupulu zako zonse. Uthenga wabwino wa kuchotsa machimo ako onse ndi wamuyaya. Chikondi Changa pa iwe ndi chamuyayanso.” 
Yesu anauza Petro ndi ophunzira kuti, “Ngati sindikusambitsa iwe ulibe cholandira pamodzi ndi Ine.” Chifukwa chimene Iye analankhulira za uthenga wabwino umenewu mu Yohane mutu wa 13 chinali chakuti kunali kofunika kwa athu kuti abadwe mwatsopano mwa madzi ndi Mzimu Woyera. Kodi inu mukukhulupilira zimenezi?
Mu ndime ya 9-10, “Simoni Petro ananena ndi Iye, Ambuye, si mapazi anga okha, komanso manja ndi mutu. Yesu ananena naye, Amene anatha kusamba alibe kusowa koma kusamba mapazi, koma ayera monse.”
Okondedwa anzanga, kodi inu mudzachita machimo ‘a thupi’ m’tsogolo, kapena simudzachita? Inu ndithudi mudzachita. Koma Yesu ananena kuti Iye adatsuka kale ngakhale machimo a m’tsogolo, mphulupulu zonse za thupi lathu ndi ubatizo Wake ndi mwazi ndipo Iye anauza ophunzira Wake momveka bwino mau a choonadi, a uthenga wabwino wa chiombolo Asanapachikidwe.
Chifukwa chakuti ife timakhala m’thupi lathu ndi zofooka zathu, ife sitingadzithandize koma kuchimwa. Yesu anatsuka machimo onse a dziko lapansi ndi ubatizo Wake. Iye sanasambitse kokha mutu wathu ndi thupi, koma wasambitsanso mapazi athu, machimo athu onse a m’tsogolo. Uwu ndi uthenga wabwino wa kubadwa mwatsopano, Ubatizo wa Yesu.
Yesu atabatizidwa, Yohane Mbatizi anachitira umboni kuti, “Onani Mwanawankhosa wa Mulungu(God) amene achotsa tchimo lake la dziko lapansi!” (Yohane 1:29) Ife tiyenera kukhulupilira kuti machimo onse a dziko lapansi atsukidwa poperekedwa kwa Yesu pamene Iye anabatizidwa.  
Pokhala m’dziko lino lapansi, anthu sangadzithandize koma kuchimwa. Ife tiyenera kuvomereza izi monga choonadi chotsiriza. Nthawi iliyonse pamene kufooka kwa thupi lathu kuwonekera, tiyenera kudzikumbutsa tokha kuti Yesu anatsuka machimo athu onse ndi machimo onse a dziko lapansi kudzera mu uthenga wabwino wa ubatizo ndi kulipirira iwo ndi mwazi Wake. Ife tiyenera kupereka mathokozo kwa Iye kuchokera pansi pa mitima yathu. Tiyeni tivomereze ndi Chikhulupiriro kuti Yesu ndi Mpulumutsi wathu komanso God wathu. Yamikani Ambuye.
Aliyense m’dziko lino lapansi amachimwa ndi thupi. Anthu amachimwa ndi thupi moyo wawo wonse, ndipo amafa. Anthu amachimwa mopitilira ndi thupi lawo.
 
 
Maganizo Oipa M’mitima ya Anthu
 
Kodi ndi chiyani chimene chimadetsa munthu?
Mitundu yosiyanasiyana ya machimo ndi maganizo oipa
 
Yesu akunena mu Mateyu 15:19-20. “Pakuti mumtima muchokera maganizo oipa, zakupha, zachigololo, zachiwerewere, zakuba, za umboni wonama, zamwano; izi ndizo ziipitsa munthu, koma kudya osasamba manja sikuipitsa munthu ai.” Chifukwa chakuti mitundu yosiyanasiyana ya machimo mu mtima mwa munthu imadetsa iwo, iwo ndi odetsedwa.
 
 
Munthu Ayenera Kuzindikira Chikhalidwe Chake Choipa
 
Kodi mu mtima mwa munthu aliyense muli chiyani? 
Mitundu khumi ndi iwiri ya machimo (Marko 7:21-23)
 
Ife tiyenera kutha kunena kuti, “Mitundu khumi ndi iwiri ya machimo imeneyo ili m’mitima ya anthu. Ndili nayo yonse mu mtima mwanga. Ndili ndi mitundu khumi ndi iwiri ya machimo mkati mwanga yomwe yalembedwa m’Baibulo.” Tisanabadwe mwatsopano mwa madzi ndi Mzimu Woyera, tiyenera kuvomereza machimo ali m’mitima mwathu. Tiyenera kuzindikira kuti ndife ochimwa otheratu pamaso pa God. Koma sitimachita zimenezo kawirikawiri. Ambiri a ife timakonda kuwiringula za machimo athu, kunena kuti, “Sindidakhalepo ndi maganizo otero mu mtima mwanga, ndinangosocheretsedwa kwa kanthawi.”
Koma kodi Yesu ananena chiyani zokhudza anthu? Iye momveka bwino ananena kuti chimene chimaturuka mkati mwa mtima wa munthu ‘chimawadetsa’ iwo. Iye anatiuza ife kuti anthu ali ndi maganizo oipa mkati mwao. Kodi inu mukuganiza bwanji? Kodi ndinu abwino kapena oipa? Kodi inu mukudziwa kuti aliyense ali ndi maganizo oipa? Inde, maganizo a aliyense ndi oipa.
Kale kwambiri, nyumba ya Sitolo la Sampoong mu Seoul inagwa mwadzidzidzi. Mabanja amene anataya okondedwa awo anali mu ululu waukulu. Koma anthu ambiri anapita kumeneko kuti akasangalale ndi chithunzi chosautsa chimenecho.
Ena anaganiza kuti, ‘Kodi amwalira angati? 200? Ayi, icho ndi chiwerengero chochepa kwambiri. 300? Mwina? Chabwino, zikanakhala zosangalatsa kwambiri komanso zochititsa chidwi ngati chiwerengero cha omwalira chikadakhala chosachepera chikwi.’ Mitima ya anthu ingakhale yoipa choncho. Ife tiyenera kuvomera icho. Zinali zosapanga ulemu bwanji kwa akufa! Zinali zowononga kwambiri bwanji kwa mabanja! Ena anawonongeka pachuma. 
Momveka bwino, anthu ena amene anabwera kudzaona ngozi imeneyi sanali a chisoni kwambiri. ‘Zikanakhala zosangalatsa kwambiri ngati ambiri akanamwalira! Chiwonenetsero chotani nanga! Bwanji nanga zomwezi zikanachitika ku bwalo la masewero lodzadza ndi anthu? Anthu zikwi zikwi akanakwiriridwa pansi pa dzidina, kodi iwo sakanakwiriridwa? Oh, inde! Izo makamaka zikanakhala zosangalatsa kwambiri kuposa izi!’ Mwina ena adali ndi maganizo monga amenewa.
Ndipo ife tonse tikudziwa momwe anthu nthawi zina angakhalire oipa. Kumene, iwo sanganene maganizo oipa otero mokweza. Akhoza kumadula malirime awo ndi kusonyeza chifundo chawo, koma mobisa, m’mitima mwawo, amalakalaka kuti chikhale chochititsa chidwi kwambiri. Iwo akufuna kuona masoka oopsa pamene zikwi za anthu aphedwa bola ngati izi sizikutsutsana ndi zofuna zawo. Ndi momwe mitima ya anthu imagwirira ntchito. Ambiri a ife tili monga chonchi tisanabadwe mwatsopano.
 
 
Kupha mu Mtima mwa Munthu Aliyense
 
Kodi ife chimachimwa chifukwa chiyani?
Chifukwa chakuti ife tili ndi maganizo oipa mu mtima mwathu. 
 
God anatiuza ife kuti muli kupha mkati mwa mtima wa munthu aliyense. Koma ambiri angakane icho. “Inu munganene bwanji zimenezo? Ndilibe maganizo aliwonse akupha mu mtima mwanga! Kodi inu komwenkomwe munganize bwanji zinthu zotero!” Iwo sadzavomereza konse kuti iwo ali ndi kupha m’mitima mwao. Iwo amaganiza kuti akupha ndi mtundu wina wa anthu.
“Wakupha anthu ambiri mu tsamba la nkhani tsiku linalilo, anthu amene anapha komanso kuotcha anthu m’chipinda chawo chapansi, iwo ndi amene ali ndi kupha m’mitima mwao! Iwo ndi mtundu wina wa anthu. Sindingakhale konse ngati iwo! Iwo ndi anthu oyipa! Akupha!” Iwo amakwiya ndi kufuula kuti, “Iwo obadwa mbeu yoipa ayenera kuchotsedwa padziko lino lapansi! Iwo onse ayenera kugamulidwa kuti aphedwe!”
Koma mwatsoka, ganizo lakupha lili mkati mwa mitima ya okwiya amenewo komanso m’mitima ya akhupha anthu ambiri mwankhanza ndi akhupha. God akutiuza ife kuti m’mitima ya anthu onse, muli kupha. Ife tiyenera kuvomera mau a God, amene amaona mpaka mkati mwathu. Ife tiyenera kubvomereza kuti, “Ndine wochimwa wokhala ndi kupha mu mtima mwanga.”
Inde, God anatiuza ife kuti muli maganizo oipa, kuphatikiza kupha, mkati mwa mitima ya anthu onse. Tiyeni tivomere mau a God. Pamene mibadwo ya anthu ikukhala yoipa kwambiri, mitundu yonse ya zipangizo zodzitetezera zikukhala zipangizo zophera. Ichi ndi chifukwa chakuti muli kupha m’mitima mwathu. Inu mungaphe chifukwa cha mkwiyo waukali, kapena mantha. Sindikunena kuti aliyense wa ife adzapha ena kwenikweni, koma kuti tili ndi maganizo otero m’mitima mwathu.
Chifukwa chakuti anthu amabadwa ndi maganizo oipa, ife tonse tili nawo m’mitima mwathu. Ena indedi amaphadi, osati chifukwa chakuti iwo amabadwa akupha, koma chifukwa tonse a ife ndi othekera kukhala akupha. God amatiuza ife kuti tili ndi maganizo oipa ndi kupha m’mitima mwathu. Ndi zoona. Palibe wa ife amene ndi opatulidwa ku choonadi chimenechi.
Choncho, njira yoyenera kuti ife titsate ndi kuvomereza mau a God ndi kumvera. Ife timachimwa m’dziko lino lapansi chifukwa chakuti ife tili ndi maganizo oipa m’mitima mwathu.
 
 
Chigololo mu Mtima Mwathu
 
God akunena kuti muli chigololo mu mtima mwa munthu aliyense. Kodi inu mukuvomera? Kodi inu mukuvomereza kuti muli ndi chigololo mu mtima mwanu? Inde, muli chigololo mu mtima mwa munthu aliyense.
Icho ndi chifukwa chake uhule ndi milandu ya zogonana ikukula m’mudzi mwathu. Ndi njira imodzi yodziwikiratu yopangira ndalama mu nyengo iliyonse m’mbiri. Malonda ena angakumane ndi mavuto a nkhawa za chuma, koma malonda oipa amenewa sakumana ndi mavuto kwambiri chifukwa chakuti muli chigololo chokhazikika m’mitima mwa anthu onse.
 
 
Chipatso cha Ochimwa Ndi Uchimo
 
Kodi munthu amafanizidwa ndi chiyani?
Mtengo umene umabala chipatso cha uchimo
 
Monga mitengo yama apulo imabala ma apulo, mitengo ya peyala mapeyala, mitengo yamadeti, madeti, ndi mitengo ya kanjedza kanjedza, ife, amene ndi obadwa ndi mitundu 12 ya machimo m’mitima mwathu, timabala chipatso cha uchimo.
Yesu amanena kuti chimene chimatuluka mu mtima wa munthu chimawadetsa iwo. Kodi inu mukugwirizana? Ife tingangogwirizana ndi mau a Yesu ndi kunena kuti, “Inde, ndife mbeu ya ochimwa, ochita zoipa. Inde, Inu muli kulondola, Ambuye.” Inde, tiyenera kuvomereza kuyipa kwathu. Tiyenera kuvomereza choonadi kwa ife eni pamaso pa God.
Monga Yesu Kristu anamvera chifuniro cha God, ife tiyenera kuvomera mau a God ndi kumvera Iye. Ndi njira yokhayo imene ife tingapulumutsidwire ku machimo athu onse kudzera m’madzi ndi Mzimu Woyera. Izi ndi mphatso zochokera kwa God.
Dziko langa ndi lodalitsidwa ndi nyengo zinayi zokongola. Ndipo pamene nyengo zikupitilira, mitundu yosiyanasiyana ya mitengo imabala zipatso zake. Momwemonso, machimo khumi ndi awiri m’mitima mwathu agwiririra pa ife ndipo mosalekeza amatitsogolera ife kuti tichimwe. Lero, kungakhale kupha kumene kwagwiririra pa mitima yathu, mawa chingakhale chigololo.
Kenako tsiku lotsatira, maganizo oipa, kenako zachiwerewere, kuba, umboni wonama, ndi zina zotero. Ndipo ife timapitiriza kuchimwa chaka chonse, mwezi uliwonse, tsiku lililonse, ora lililonse. Tsiku silitha popanda kuchimwa kwathu tchimo linalake. Ife timapitiriza kulumbira kuti tichoka ku uchimo, koma ife sitingadzithandize koma kuchimwa chifukwa chakuti ndife obadwa motere.
Kodi inu munaonapo mtengo wa apulo ukukana kubala ma apulo chifukwa chakuti uwo sukufuna? “Sindikufuna kubala ma apulo!” Ngakhale uwo utapanga maganizo kuti ukane kubala chipatso, kodi uwo sungabale bwanji ma apulo? Maluwa adzaphukira mu nyengo ya kuturuka, ma apulo adzakula ndi kupsa mu nthawi yotentha, ndipo chipatso chidzakhala chokonzeka kutoledwa ndi kudyedwa mu nthawi yozizira.
Ndi ndondomeko ya chilengedwe, ndipo moyo wa ochimwa uyeneranso kutsata ndondomeko ya chilengedwe. Ochimwa sangadzithandize koma kubala zipatso za uchimo.
 
 

‘Ubatizo ndi Mtanda wa Yesu’ Zinali Zotetezera Machimo Athu

 
Kodi mau akuti chitetezero akutanthauza chiyani?
Ndi kulipira kwa mphotho ya uchimo kudzera mu Ubatizo wa Yesu (kuika manja) ndi mwazi Wake pa Mtanda.
 
Tiyeni tiwerenge ndime ya m’Baibulo kuti tipeze momwe ochimwa, ana ocita zoipa, angachitire chitetezero cha machimo awo pamaso pa God ndi kukhala moyo wawo mwachimwemwe. Ichi ndi uthenga wabwino wa chitetezero cha machimo.
Mu Levitiko 4, kwanenedwa kuti, “Ndipo akachimwa wina wa anthu a m’dziko, osati dala, pa china cha zinthu zilizonse aziletsa Yehova, napalamula; akamdziwitsa kuchimwa kwake adachimwako, azidza nacho chopereka chake mbuzi yaikazi, yopanda chilema, chifukwa cha kuchimwa kwake adakuchita. Aike dzanja lake pamutu pa nsembe yauchimo, naiphe nsembe yauchimo pamalo pa nsembe yopsereza. Ndipo wansembe atengeko mwazi ndi chala chake, nauike pa nyanga za guwa la nsembe yopsereza, ndi kuthira mwazi wake wonse patsinde pa guwa la nsembe. Nachotse mafuta ake onse, monga umo amachotsera mafuta pa nsembe yoyamika; ndipo wansembeyo awatenthe paguwa la nsembe akhale fungo lokoma la kwa Yehova; ndi wansembe amchitire chomtetezera, ndipo adzakhululukidwa (kuchotsedwa).” (Levitiko 4:27-31)
M’masiku a Chipangano Chakale, kodi anthu ankatetezera bwanji machimo ao? Iwo ankaika manja awo pamutu pa nsembe yauchimo ndi kupititsira machimo awo kwa iyo.
Kwalembedwa mu Levitiko. “Lankhula ndi ana a Israele, nunene nao, Aliyense mwa inu akabwera nacho chopereka cha kwa Yehova, muzibwera nacho chopereka chanu chikhale cha zoweta, cha ng’ombe, kapena cha nkhosa, kapena cha mbuzi. Chopereka chake chikakhala nsembe yopsereza ya ng’ombe, azibwera nayo yaimuna yopanda chilema; (apereke iyo mwaufulu wake pa khomo la chihema chokomanako pamaso pa Yehova—NKJV). Ndipo aike dzanja lake pamutu pa nsembe yopsereza; ndipo idzalandiridwa m’malo mwake, imtetezere.” (Levitiko 1:2-4)
God anapanga iwo kukonza nsembe ya uchimo imene imagwiritsidwa ntchito kutetezera machimo a Israeli. Ndipo Iye anawauza kuti ‘aike manja awo’ pa mutu wa nsembe ya machimo, kuti apititsire machimo. Mkati mwa bwalo la Chihema chopatulika, munali guwa la nsembe yopsereza. Linali bokosi lalikulu pang’ono kuposa tebulo la nsanja ndipo linali ndi nyanga pa ngodya zinayi. Anthu a Israeli ankatetezera machimo awo popititsira machimo awo pa mutu wa nsembe ya machimo ndi kutentha nyama yake pa guwa la nsembe yopsereza.
God ananena mu Levitiko kwa anthu kuti “apereke iyo mwaufulu wake pa khomo la chihema chokomanako pamaso pa Yehova.” Machimo ao ankaperekedwa pa nsembe ya uchimo pamene iwo aika manja ao pa mutu wake, ndipo kenako ochimwa ankadula khosi la nyama ya nsembeyo kuti aphe iyo. Ndipo ansembe ankaika mwazi wake pa nyanga za guwa la nsembe yopsereza.
Pambuyo pake, thupi la nsembe linatsukidwa ziwalo zake zamkati, ndipo nyama yake inadulidwa mzidutswa ndi kutentha mpaka phulusa pa guwa la nsembe yopsereza. Kenako fungo lokoma la nyamayo linaperekedwa kwa God kuti apereke chitetezero chawo. Umu ndi momwe ankatetezera machimo awo a tsiku ndi tsiku.
Kenako kunali nsembe ya chitetezero cha machimo awo a pachaka. Iyo inkasiyana ndi nsembe ya chitetezero cha machimo a tsiku ndi tsiku mwakuti mkulu wansembe ankaika manja ake pa nsembe ya uchimo m’malo mwa anthu onse a Israeli ndipo iye ankawaza mwazi ku m’mawa kwa chotetezerapo kasanu ndi kawiri. Komanso, kuika manja pa mutu wa mbuzi yamoyo kunkachitidwa pamaso pa anthu a Israeli pa tsiku la khumi la mwezi wa chisanu ndi chiwiri chaka chilichonse (Levitiko 16:5-27).
 
Kodi ndindani amaimilira nsembe ya uchimo ya m’Chipangano Chakale?
Yesu Kristu 
 
Tsopano, tiyeni tione momwe ndondomeko ya kaperekedwe ka nsembe inasinthira m’Chipangano Chatsopano komanso momwe lamulo la God la muyaya lakhalira losasintha kwa zaka.
Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu anayenera kufa pa Mtanda? Kodi Iye analakwa chiyani pa dziko lino lapansi kuti God adalola Mwana Wake kufa pa Mtanda? Kodi ndindani anamukakamiza Iye kufa pa Mtanda? Pamene ochimwa onse a dziko lapansi, kutanthauza ife tonse, tidagwera mu uchimo, Yesu anadza ku dziko lino lapansi kudzatipulumutsa ife.
Iye anabatizidwa ndi Yohane Mbatizi pa Yordano ndi kutenga chilango pa Mtanda cha machimo onse m’malo mwa mtundu wonse wa anthu. Momwe Yesu anabatizidwira, momwe Iye anakhetsera mwazi pa Mtanda zinali monga nsembe ya chitetezero ya m’Chipangano Chakale, kuika manja pa nsembe ya uchimo ndi kukhetsa kwake kwa mwazi.
Umu ndi momwe zinkachitidwira m’Chipangano Chakale. Wochimwa ankaika manja pa nsembe ya uchimo ndi kuvomereza machimo ake, kunena kuti, “Ambuye, ndachimwa. Ndapha ndi kuchita chigololo.” Kenako machimo ake ankaperekedwa pa nsembe ya uchimo.
Ndipo monga wochimwa ankadula khosi la nsembe ya uchimo ndi kupereka iyo pamaso pa God, Yesu anaperekedwa mu njira yomweyo kuti atetezere machimo athu onse. Yesu anabatizidwa ndi kukhetsa mwazi pa Mtanda kudzapulumutsa ife ndi kutetezera machimo athu onse kudzera mu nsembe Wake.
Kwenikweni, Yesu anafa chifukwa cha ife. Pamene ife taganizira icho, kodi tanthauzo linali chiyani loperekera nyama zopanda chirema zimenezo monga nsembe za machimo onse a anthu? Kodi nyama zonse zimenezo zinkadziwa kuti uchimo unali chiyani? Nyama sizidziwa uchimo. Izo sizinkatha kuchotsa machimo a anthu onse.
Monga momwe nyama zimenezo zinalibiretu chirema, chimodzimodzinso Yesu analibe uchimo. Iye ndi God Woyera, Mwana wa God, ndipo Iye sanachimwepo. Choncho, Iye anatenga machimo athu onse kudzera mu ubatizo Wake mu Yordano pamene Iye anali ndi zaka 30.
Kunali kuti atenge machimo athu onse, ndipo Iye anafa pa Mtanda chifukwa cha machimo amene Iye anatenga kwa ife. Unali utumiki Wake wa chipulumutso umene unatsuka machimo onse a mtundu wa anthu. Kwalembedwa mu Mateyu 3.
 
 
Chiyambi cha Uthenga Wabwino wa Chitetezero cha Machimo
 
Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu anabatizidwa ndi Yohane Mbatizi mu Yordano? 
Kuti akwaniritse chilungamo chonse
 
Tsopano, kwalembedwa mu Mateyu 3 kuti, “Pamenepo Yesu anachokera ku Galileya nadza ku Yordani kwa Yohane, kudzabatizidwa ndi iye. Koma Yohane anati amkanize, nanena, Ndiyenera ine kubatizidwa ndi Inu, ndipo Inu mudza kwa ine kodi? Koma Yesu anayankha, nati kwa iye, Balola tsopano: pakuti kuyenera ife kukwaniritsa chilungamo chonse motero.” (Mateyu 3:13-15)
Ife tiyenera kudziwa ndi kumvetsetsa chifukwa chimene Yesu anabatizidwira pamene Iye anali ndi zaka 30. Iye anabatizidwa kuti atetezere machimo a anthu onse ndi kukwaniritsa chilungamo chonse cha God. Kuti apulumutse anthu onse ku machimo awo, Yesu Kristu, Iye wopanda chirema, anabatizidwa Yekha ndi Yohane Mbatizi.
Motero, Iye anatenga machimo a dziko lapansi ndi kudzipereka Yekha kuti atetezere machimo a anthu onse. Kuti tipulumutsidwe ku uchimo, ife tiyenera tonse kudziwa choonadi ndi kukhulupilira mu choonadi. Zili kwa ife kukhulupilira mu chipulumutso Wake ndi kupulumutsidwa.
Kodi ubatizo wa Yesu umatanthauza chiyani? Ndi chimodzimodzi ndi kuika manja m’Chipangano Chakale. Mu Chipangano Chakale, machimo a anthu onse ankaperekedwa pa mutu wa nsembe ya uchimo poika manja. Chimodzimodzinso, m’Chipangano Chatsopano, Yesu anatenga machimo onse a dziko lapansi podzipereka Yekha monga nsembe ya uchimo ndi kubatizidwa ndi Yohane Mbatizi.
Yohane Mbatizi anali munthu wamkulu kwambiri pakati pa anthu onse, woimirira wa mtundu wa anthu woikidwa ndi God. Monga woimirira wa mtundu wa anthu, mkulu wansembe wa onse, iye anaika manja ake pa Yesu ndi kupititsira machimo onse a dziko lapansi kwa Iye. ‘Ubatizo’ umatanthauza, ‘kupatsira, kuikidwa, ndi kutsukidwa’.
Kodi mukudziwa chifukwa chimene Yesu anadzera ku dziko lino lapansi ndi kubatizidwa ndi Yohane Mbatizi? Kodi mukhulupirira mwa Yesu podziwa tanthauzo la ubatizo wa Yesu? Ubatizo wa Yesu unali wochotsa machimo athu onse, machimo amene ife, ana ocita zoipa, timachita ndi thupi lathu moyo wathu wonse. Yesu anabatizidwa ndi Yohane Mbatizi kuti akwaniritse uthenga wabwino woyambirira wa chitetezero cha machimo athu onse.
Mu Mateyu 3:13-17, kwalembedwa kuti, ‘Pamenepo’, ndipo zikutanthauza kuti nthawi imene Yesu anabatizidwa, ndi nthawi imene machimo onse a dziko lapansi anaperekedwa pa Iye.  
‘Pamenepo’ Yesu anachotsa machimo onse a mtundu wa anthu, anafa pa Mtanda patapita zaka zitatu, ndipo anaukitsidwa patapita masiku atatu. Kuti atsuke machimo onse a dziko lapansi, Iye anabatizidwa kamodzi kokha, kufa pa Mtanda kamodzi kokha, ndipo anauka kwa akufa kamodzi kokha. Kwa iwo onse amene akufuna kuomboledwa ku machimo awo pamaso pa God, Iye anapulumutsa iwo onse kamodzi kokha.
Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu anayenera kubatizidwa? Kodi ndi chifukwa chiyani Iye anayenera kuvala kolona wa minga ndi kuweruzidwa m’bwalo la Pilato monga chigawenga wamba? Kodi ndi chifukwa chiyani Iye anayenera kupachikidwa pa Mtanda ndi kukhetsa mwazi mpaka imfa? Chifukwa cha zonse zili pamwambapa ndi chakuti Iye anatenga machimo onse a dziko lapansi, machimo a inu ndi ine, pa Iye Mwini kudzera mu ubatizo Wake. Ndipo chifukwa cha machimo athu, Iye adayenera kufa pa Mtanda.
Ife tiyenera kukhulupilira m’mau a chipulumutso akuti God watipulumutsa ife ndi kukhala othokoza kwa Iye. Popanda ubatizo wa Yesu, Mtanda Wake, ndi kuuka Wake, sikukanakhala chipulumutso kwa ife.
Pamene Yesu anabatizidwa ndi Yohane kuti achotse machimo onse a dziko lapansi, Iye anatenga machimo athu onse ndipo motero kutipulumutsa ife amene timakhulupilira mu uthenga Wake wabwino wa chipulumutso. Kuli anthu amene amaganiza kuti, ‘Koma Iye anachotsa kokha uchimo woyambirira, sichoncho?’ Koma iwo akulakwitsa.
Kwalembedwa momveka bwino m’Baibulo kuti Yesu anatenga machimo onse a dziko lapansi kamodzi kokha pamene Iye anabatizidwa. Machimo athu onse, kuphatikiza uchimo woyambirira, watsukidwa. Kwalembedwa mu Mateyu 3:15 kuti, “Pakuti kuyenera ife kukwaniritsa chilungamo chonse motero.” Kukwaniritsa chilungamo chonse kukutanthauza kuti machimo onse, mosachotsera, achotsedwa kwa ife.
Kodi Yesu watsukanso machimo a moyo wathu wonse? Inde, Iye watero. Tiyeni tipeze umboni wa icho mu Levitiko choyamba. Ikutiuza ife za mkulu wansembe ndi nsembe ya Tsiku la Chitetezero.
 
 
Nsembe ya Chitetezero cha Machimo a Chaka ndi Chaka a Aisraeli Onse
 
Kodi Aisraeli ankakhoza kusunga chiyero nthawi zonse kudzera mu nsembe ya uchimo ya dziko lapansi lino?
Konse ayi
 
“Aroni abwere nayo ng’ombe ya nsembe yauchimo, ndiyo yakeyake, nachite chodzitetezera iye yekha, ndi mbumba yake. Ndipo atenge mbuzi ziwirizo naziimike pamaso pa Yehova pakhomo pa chihema chokomanako. Ndipo Aroni ayese maere pa mbuzi ziwirizo; maere amodzi kwa Yehova, ndi amodzi kwa Azazele. Ndipo Aroni abwere nayo mbuzi imene adaigwera maere a Yehova, naiyese nsembe yauchimo. Koma mbuzi imene adaigwera maere a Azazele, aiike yamoyo pamaso pa Yehova, kuti achite nayo chotetezera, kuitumiza kuchipululu ikhale ya Azazele.” (Levitiko 16:6-10) Apa Aroni anatenga mbuzi ziwiri pakhomo pa chihema chokomanako kuti atetezere machimo a chaka ndi chaka a Aisraeli.
“Ndipo Aroni ayese maere pa mbuzi ziwirizo; maere amodzi kwa Yehova, ndi amodzi kwa Azazele.” Mbuzi ya azazeli inkafunika ku chitetezero.
Mosiyana ndi izi, nsembe ya chitetezero cha machimo a tsiku ndi tsiku, imene wochimwa ankaika manja ake pa mutu wa chopereka kuti apereke machimo ake. Koma ku machimo a pa chaka a Aisraeli, mkulu wansembe, m’malo mwa anthu onse, ankapereka machimo a pa chaka pa nsembe ya uchimo pa tsiku la khumi la mwezi wa chisanu ndi chiwiri chaka chilichonse.
Mu Levitiko 16:29-31, kwalembedwa kuti, “Ndipo lizikhala kwa inu lemba losatha; mwezi wachisanu ndi chiwiri, tsiku lakhumi la mweziwo, muzidzichepetsa, osagwira ntchito konse, kapena wa m’dziko, kapena mlendo wakukhala pakati panu; popeza tsikuli adzachitira inu chotetezera, kukuyeretsani; adzakuyeretsani, kukuchotserani zoipa zanu zonse pamaso pa Yehova. Likhale kwa inu Sabata lakupumula, kuti mudzichepetse; ndilo lemba losatha.” (Levitiko 16:29-31)
Mu Chipangano Chakale, anthu a Israeli ankabweretsa nsembe ya uchimo kuti atetezere machimo a tsiku ndi tsiku ndi kupereka machimo awo pa mutu wake, kuvomereza kuti, “Ambuye, ndachita tchimo lotero ndi lotero.” Kenako iye ankadula khosi la nsembe ya uchimo, ndi kupereka mwazi kwa wansembe, ndi kupita kunyumba, kutsimikiza kuti iye tsopano anali omasuka ku machimo ake. Nsembe ya uchimo inkafera ochimwa, ndi uchimo pa mutu pake. Nsembe ya uchimo inkaphedwa m’malo mwa wochimwa. Mu Chipangano Chakale, nsembe ya uchimo inkakhala mbuzi, mwana wa ng’ombe, ng’ombe ya mphongo, zonse zopanda chirema ndi nyama zoyera zimene God anazisiyanitsa.
M’malo moti wochimwa afe chifukwa cha machimo Wake, God, mu chifundo Chake chosatha, analola kuti moyo wa nyama uperekdwe m’malo mwake.
Mwanjira yotere mu Chipangano Chakale, ochimwa ankatha kutetezera machimo awo kudzera mu nsembe ya chitetezero. Zolakwa za wochimwa zinkaperekedwa pa nsembe ya uchimo poika manja, ndipo mwazi wake unkaperekedwa kwa wansembe kuti utetezere machimo a wochimwa.
Komabe, zinali zosatheka kutetezera machimo tsiku lililonse. Choncho, God analola mkulu wansembe kutetezera machimo a chaka chonse, chaka chilichonse pa tsiku la khumi la mwezi wa chisanu ndi chiwiri, m’malo mwa anthu onse a Israeli.
Nanga kodi ntchito ya Mkulu Wansembe pa Tsiku la Chitetezero inali chiyani? Choyamba, Aroni mkulu wansembe ankaika manja ake pa nsembe ya uchimo, kuvomereza machimo a anthu kuti, “Ambuye, anthu a Israeli achita machimo otero ndi otero: kupha, chigololo, zachiwerewere, kuba, umboni wonama, mwano...”
Kenako, iye anadula khosi la nsembe ya uchimo, kutenga mwazi umene unawazidwa kasanu ndi kawiri pa chotetezerapo mkati mwa chihema chopatulika chokomanako. (Mu Baibulo, nambala 7 imatengedwa kukhala nambala yangwiro.)
Inali ntchito yake kupereka machimo a pa chaka a anthu pa mutu wa nsembe ya uchimo m’malo mwa Aisraeli onse, ndipo nsembe ya uchimo inkaperekedwa m’malo mwawo.
Chifukwa chakuti God ndi wolungama, kuti apulumutse anthu onse ku machimo awo, Iye analola nsembe ya uchimo kufa m’malo mwa anthu. Chifukwa chakuti God ndi wachifundo, Iye ankalola anthu kupereka moyo wa nyama ya nsembe m’malo mwawo. Kenako mkulu wansembe anawaza mwazi mbali ya kum’mawa ya chotetezerapo ndipo motero anachita chitetezero cha machimo onse a Aisraeli a chaka chatha pa Tsiku la Chitetezero, pa tsiku lakhumi la mwezi wachisanu ndi chiwiri.
 
Kodi Mwanawankhosa wa nsembe malingana ndi Chipangano Chakale ndindani?
Yesu amene ndi opanda chirema
 
Mkulu wansembe ankayenera kupereka mbuzi ziwiri pa Tsiku la Chitetezero za anthu a Israeli. Imodzi ya izo inkatchedwa mbuzi ya azazeli imene ikutanthauza ‘kutulutsa’. Mu njira yomweyo, mbuzi ya azazeli ya Chipangano Chatsopano ndi Yesu Kristu. “Pakuti Mulungu(God) anakonda dziko lapansi kotero, kuti anapatsa Mwana wake wobadwa yekha, kuti yense wakukhulupirira Iye asatayike, koma akhale nao moyo wosatha.” (Yohane 3:16)
God anatipatsa ife Mwana Wake yekha monga Mwanawankhosa wa nsembe. Ndipo monga Mwanawankhosa wa nsembe wa mtundu wonse wa anthu, Iye anabatizidwa ndi Yohane Mbatizi ndi kukhala Mpulumutsi, Mesiya wa dziko lapansi. Mesiya amatanthauza ‘Mpulumutsi’, ndipo Yesu Kristu amatanthauza ‘Mfumu imene yadza kudzatipulumutsa ife’.
Choncho, monga machimo a chaka ndi chaka a Aisraeli ankatetezeredwa pa Tsiku la Chitetezero m’Chipangano Chakale, Yesu Kristu, pafupifupi zaka 2000 zapitazo, anadza ku dziko lino lapansi kudzabatizidwa ndi kukhetsa mwazi mpaka imfa pa Mtanda kuti atsirize uthenga wabwino wa chitetezero cha machimo athu onse.
Pa nthawi ino, tiyeni tiwerenge ndime mu Levitiko. “Aroni aike manja ake onse awiri pamutu pa mbuzi yamoyo, ndi kuvomereza pa iyo mphulupulu zonse za ana a Israele, ndi zolakwa zao zonse, monga mwa zochimwa zao zonse; naike izi pamutu pa mbuziyo, ndi kuitumiza kuchipululu ndi dzanja la munthu wompangiratu, ndi mbuziyo isenze yokha mphulupulu zonsezo kunka nazo ku dziko la pa lokha; ndipo azitaya mbuziyo m’chipululu.” (Levitiko 16:21-22)
Kwalembedwa kuti machimo a anthu onse ankaikidwa pa mutu wa mbuzi monga kwanenedwanso mu Levitiko 16. ‘Zolakwa zao zonse’ zikutanthauza machimo onse amene iwo anachita m’mitima mwao, machimo onse amene iwo anachita ndi thupi lao. Ndipo ‘zolakwa zao zonse’ zinkaikidwa pa mutu wa nsembe ya uchimo poika manja.
 
 
Kudzera mu Lamulo la God, Tiyenera Kukhala ndi Chidziwitso Choona cha Machimo Athu Onse
 
Kodi ndi chifukwa chiyani God anatipatsa ife Lamulo?
Kuti atipatse ife chidziwitso cha uchimo
 
Chilamulo ndi malamulo a God ali ndi ndime 613. Kwenikweni, pamene ife taganizira icho, ife tachita zimene Iye anatiuza ife kuti tisachite ndipo sitinachite zimene Iye anatiuza kuti tichite.
Choncho, ndife ochimwa. Ndipo kwalembedwa m’Baibulo kuti God anatipatsa ife malamulo amenewo kuti ife tizindikire machimo athu (Aroma 3:20). Zikutanthauza kuti Iye anatipatsa ife Lamulo Wake ndi malamulo Wake kuti atiphunzitse ife kuti ndife ochimwa. Iye sanatipatse ife iwo chifukwa chakuti ndife othekera kusunga iwo, koma kwa ife kuti tidziwe machimo athu.
Iye sanatipatse ife Chilamulo Wake ndi malamulo kuti ife tisunge. Inu simungayembekezere galu kuti akhale ngati munthu. Munjira yomweyo, ife sitingakhale konse mwa lamulo la God koma tingazindikire kokha machimo athu kudzera mu Chilamulo Wake ndi malamulo.
God anatipatsa ife Lamulo, chifukwa chakuti ife tokha sitizindikira kuti ndife mulu wa uchimo. “Ndinu akupha, achiwerewere, ochita zoipa.” Iye anatiuza ife kuti tisaphe, koma ife timaphabe m’mitima mwathu ndipo nthawi zina pochita.
Komabe, chifukwa kwalembedwa mu Chilamulo kuti ife sitiyenera kupha, ife tikudziwa kuti ndife akupha, kunena kuti, “Ah ndinalakwitsa. Ndine wochimwa chifukwa chakuti ndinachita chinachake chimene sindikuyenera kuchita. Ndachimwa.”
Choncho, kuti apulumutse anthu a Israeli ku uchimo, God analola Aroni kupereka nsembe ya chitetezero m’Chipangano Chakale, ndipo anali Aroni amene ankatetezera anthu kamodzi pa chaka.
Mu Chipangano Chakale, nsembe za uchimo ziwiri zinkayenera kuperekedwa kwa God pa Tsiku la Chitetezero. Imodzi ikaperekedwa pamaso pa God pamene inayo ikatumizidwa m’chipululu pambuyo pa kuika manja, kutenga ndi iyo machimo onse a pa chaka a Aisraeli. Mbuzi isanaperekedwe mu chipululu ndi dzanja la munthu wompangiratu, mkulu wansembe ankaika manja ake pa mutu wa mbuzi yamoyo ndi kuvomereza machimo a Israeli. “Ambuye, anthu apha, achita zachiwerewere ndi kuba komanso kupembedza mafano... Ife tachimwa.”
Chipululu ndi dziko la mchenga ndi chipululu. Mbuzi ya azazeli inkatumizidwa ku chipululu chosatha ndi kufa. Pamene iyo inkatumizidwa, anthu a Israeli ankapitiriza kuyangana iyo kufikira pamene iyo inasowa kutali, ndi kukhulupirira kuti machimo awo apita pamodzi ndi mbuzi ya azazeliyo. Anthu anapeza mtendere wa mu mtima, ndipo mbuzi ya azazeli inafa m’chipululu chifukwa cha machimo a pa chaka a Aisraeli onse. 
Ndipo God anatetezera machimo athu onse kudzera mwa Mwanawankhosa wa God, Yesu Kristu. Machimo athu onse anatsukidwa motheratu kudzera mu ubatizo wa Yesu ndi mwazi Wake pa Mtanda.
Yesu ndi God komanso Mpulumutsi wathu. Iye ndi Mwana wa God amene anadza kudzapulumutsa mtundu wonse wa anthu ku uchimo ndipo Iye ndi Mlengi amene anatipanga ife mu Chifaniziro Wake. Iye anadza ku dziko lino lapansi kudzatipulumutsa ife ku uchimo.
Osati machimo okha a tsiku ndi tsiku amene ife timachita ndi thupi lathu, koma machimonso onse m’tsogolo, machimo onse a mmaganizo ndi thupi lathu anaperekedwa pa Yesu. Motero, Iye adayenera kubatizidwa ndi Yohane Mbatizi kuti akwaniritse chilungamo chonse cha God, chitetezero chonse cha machimo a dziko lapansi.
Zaka zitatu Yesu asanapachikidwe, pamene Iye poyamba anayamba utumiki Wake wapoyera, Iye anatenga machimo onse a dziko lapansi pobatizidwa ndi Yohane Mbatizi mu Yordano. Chipulumutso Wake cha mtundu wa anthu kudzera mu chitetezero cha machimo athu onse chinayamba ndi ubatizo Wake. 
Mu Mtsinje wa Yordano, pa malo amene anali akuya pafupifupi kufika m’chiuno, Yohane Mbatizi anaika manja ake pa mutu wa Yesu ndi kumunyika Iye m’madzi. Ubatizo umenewu unali chimodzimodzi ndi kuika manja m’Chipangano Chakale ndipo unali ndi mphamvu yofanana ya kupereka machimo onse.
Kunyikidwa m’madzi kunatanthauza imfa, ndipo kuturuka m’madzi kunatanthauza kuuka. Motero, pobatizidwa ndi Yohane Mbatizi, Yesu adakwaniritsa ndi kuvumbulutsa zonse zitatu: kutenga machimo onse, kupachikidwa, ndi kuuka.
Ife tingapulumutsidwe kokha ngati timvera mau amene Yesu anatipulumutsira nao ku uchimo. God anasankha kutipulumutsa kudzera mwa Yesu, ndipo pangano limene Iye anapanga m’Chipangano Chakale lidakwaniritsidwa motero. Ndipo Yesu anayenda kupita ku Mtanda ndi machimo athu onse pa mutu Wake.
 
Kodi ndi ntchito yotani imene yatsala kwa ife popeza Yesu anafafaniza machimo athu onse?
Zonse zimene ife tiyenera kuchita ndi kukhala ndi Chikhulupiriro m’mau a God.
 
Mu Yohane 1:29, kwalembedwa kuti, “M’mawa mwake anaona Yesu alinkudza kwa iye, nanena, Onani Mwanawankhosa wa Mulungu(God) amene achotsa tchimo lake la dziko lapansi!” Yohane Mbatizi anachitira umboni kuti, “Onani Mwanawankhosa wa Mulungu(God) amene achotsa tchimo lake la dziko lapansi!” Machimo onse a mtundu wa anthu anaperekedwa pa Yesu pamene Iye anabatizidwa mu Yordano. Khulupilirani icho! Kenako inu mudzadalitsidwa ndi chitetezero cha machimo anu onse.
Ife tiyenera kukhala ndi Chikhulupiriro m’mau a God. Ife tiyenera kuika pambali maganizo athu ndi kuuma mtima kwathu, ndipo mosavuta kukhulupilira mu choonadi chakuti Yesu anatenga machimo athu a dziko lapansi, komanso kumvera mau olembedwa a God.
Kunena kuti Yesu anachotsa machimo onse a dziko lapansi, ndi kunena kuti Iye anakwaniritsa chilungamo cha God potetezera machimo athu ndi chinthu chimodzimodzi ndendende. Ndipo ‘kuika manja’ ndi ‘ubatizo’ nazonso ndizofanana.
Mosasamala kathu kuti kaya ife timanena kuti ‘zonse’, ‘chilichonse’, kapena ‘chonse’ tanthauzo limakhalabe lofanana. Tanthauzo la mau akuti, ‘kuika manja’ m’Chipangano Chakale limakhalabe lofanana m’Chipangano Chatsopano, kupatula kuti mau akuti ubatizo amagwiritsidwa ntchito m’malo mwake.
Zimabwera ku choonadi chophweka chakuti Yesu anabatizidwa komanso kuweruzidwa pa Mtanda kuti atetezere machimo athu onse. Ndipo ife timapulumutsidwa pamene tikhulupirira uthenga wabwino woyambirira uwu.
Pamene tinena kuti Yesu anachotsa ‘tchimo lake la dziko lapansi’ (Yohane 1:29), kodi tikutanthauza chiyani ndi machimo a dziko lapansi? Tikutanthauza machimo onse amene timabadwa nawo ndi mutuluka maganizo oipa, zachiwerewere, zachigololo, zakupha, zakuba, masiriro, zoipa, chinyengo, chinyanso, diso loipa, mwano, kudzikuza, kupusa zokhala m’maganizo mwathu. Zikutanthauza machimo onse oipa ndi zolakwa zathupi ndi za mtima.
“Pakuti mphotho yake ya uchimo ndi imfa; koma mphatso yaulere ya Mulungu(God) ndiyo moyo wosatha wa mwa Khristu Yesu Ambuye wathu.” (Aroma 6:23) “wopanda kukhetsa mwazi palibe kukhululukidwa (Kuchotsa) kwa machimo.” (Ahebri 9:22) Monga kwanenedwa mu ndime zimenezi, machimo onse ayenera kulipiridwa. Ndipo Yesu Kristu, kuti apulumutse mtundu wonse wa anthu ku uchimo, anapereka moyo Wake ndi kulipira mphotho ya uchimo kamodzi kokha.
Choncho, zonse zimene tiyenera kuchita ndi kukhulupirira mu Ubatizo wa Yesu ndi Mwazi Wake, uthenga wabwino woyambirira, ndi mu kukhalapo kwa Yesu ngati God wathu ndi Mpulumutsi wathu kuti timasuke ku machimo athu onse.
 
 
Chitetezero cha Machimo a Mawa
 
Kodi ife tikufunika kupereka nsembe ya machimo athu mopitilira?
Ayinso
 
Machimo a mawa ndi mkuja, komanso machimo amene ife timachita kufikira tsiku limene ife tidzafa aphatikizidwanso mu ‘tchimo lake la dziko lapansi’ monganso machimo a lero, dzulo, ndi dzana aphatikizidwanso mu ‘tchimo lake la dziko lapansi’. Machimo a anthu kuyambira kubadwa mpaka kufa onse ali mu gao la ‘tchimo lake la dziko lapansi’ ndipo uchimo wa dziko lapansi unaperekedwa pa Yesu kudzera mu ubatizo Wake. Choncho machimo onse amene ife tidzachita kufikira tsiku limene ife tidzafa achotsedwa kale kwa ife.
Ndipo ife tikufunika kokha kukhulupilira mu uthenga wabwino weniweni umenewu, mau olembedwa a God, ndi kumvera kuti tipulumutsidwe. Ife tiyenera kuika pambali maganizo athu kuti tiomboledwe ku machimo athu onse. Inu mwina mungafunse kuti, “Kodi Iye angatenge bwanji machimo amene sanachitidwe?” Ndiye, ndikufunsaninso inu, “Nthawi iliyonse imene ife tachimwa, kodi Yesu ayenera kubweranso m’dziko lino lapansi kukhetsa mwazi Wake mobwereza bwereza?”
Mkati mwa uthenga wabwino wa kubadwa mwatsopano, muli lamulo la chitetezero cha machimo. “Ndipo wopanda kukhetsa mwazi palibe (Kuchotsa) kwa machimo.” (Aheberi 9:22) Pamene munthu ankafuna kuomboledwa ku machimo ake m’masiku a m’Chipangano Chakale, iye ankayenera kupereka machimo ake poika manja pa nsembe ya uchimo, ndipo nsembe ya uchimoyo inkayenera kufera machimo ake.
Momwemonso, Mwana wa God anadza ku dziko lino lapansi kudzapulumutsa mtundu wonse wa anthu. Iye anabatizidwa kuti atenge machimo athu onse ndipo Iye anakhetsa mwazi pa Mtanda kuti alipire mphotho ya machimo athu ndipo Iye anafa pa Mtanda, kunena kuti, “Kwatha!” Iye anauka kwa akufa patatha masiku 3 ndipo tsopano akukhala ku dzanja la manja la God. Iye wakhala Mpulumutsi wathu kwamuyaya.
Kuti afafanizidwe kwathunthu machimo athu, tiyenera kutaya maganizo athu onse okhazikika ndi kusiya chikhulupiriro cha chipembedzo chakuti tiyenera kuomboledwa ku machimo athu a tsiku ndi tsiku tsiku lililonse. Kuti machimo a mtundu wa anthu afafanizidwe, nsembe inkayenera kuperekedwa, kamodzi kokha. God Kumwamba anapereka machimo onse a dziko lapansi pa Mwana Wake kudzera mu ubatizo Wake ndipo adamupanga Iye kuti apachikidwe chifukwa cha ife. Ndipo ndi kuukwa Wake kwa akufa, chipulumutso chathu chinakwaniritsidwa.
“Zoonadi Iye ananyamula zowawa zathu, ndi kusenza zisoni zathu; koma ife tinamuyesa wokhomedwa, wokanthidwa ndi Mulungu(God), ndi wovutidwa. Koma Iye analasidwa chifukwa cha zolakwa zathu, natundudzidwa chifukwa cha mphulupulu zathu...Ndipo Yehova anaika pa Iye mphulupulu ya ife tonse.” Mu Yesaya 53, kwanenedwa kuti zolakwa zonse ndi mphulupulu za dziko lapansi, za mtundu wonse wa anthu zinaperekedwa pa Yesu Kristu.
Ndipo m’Chipangano Chatsopano, mu Aefeso 1:4, kwalembedwa kuti, “Monga anatisankha ife mwa Iye, lisanakhazikike dziko lapansi.” Izi zikutiuza ife kuti Iye anatisankha ife mwa Iye lisanakhazikike dziko lapansi. Dziko lapansi lisanalengedwe, God anatisankha ife kuti atipange ife kukhala anthu Wake, olungama opanda chirema mwa Kristu. Kaya ife tidaganizapo chiyani kale, ife tiyenera tsopano kukhulupilira ndi kumvera mau a God, mau a madzi, mwazi, ndi Mzimu Woyera.
God anatiuza ife kuti Mwanawankhosa Wake, Yesu Kristu, anachotsa machimo a dziko lapansi ndi kutetezera mtundu wonse wa anthu. Mu Ahebri 10, kwalembedwa kuti, “Pakuti chilamulo, pokhala nao mthunzi wa zokoma zilinkudza, osati chifaniziro chenicheni cha zinthuzo, sichikhozatu, ndi nsembe zomwezi chaka ndi chaka, zimene azipereka kosalekeza, kuwayesera angwiro iwo akuyandikira.” (Ahebri 10:1)
Apa ikunena kuti ndi nsembe zomwezi chaka ndi chaka zimene timapereka sizikhozatu kutiyeretsa ife mwangiro. Chilamulo ndi mthunzi wa zinthu zabwino zirinkudza, osati chifaniziro cheni cheni cha zinthuzo. Yesu Kristu, Mesiya amene ankayenera kudza, anatipanga ife kukhala angwiro kamodzi kokha (monga momwe machimo a chaka ndi chaka a Aisraeli anatetezeredwa kamodzi kokha) pobatizidwa ndi kupachikidwa kuti atetezere machimo athu onse.
Choncho Yesu ananena mu Ahebri 10 kuti, “Pamenepo anati, Taonani, ndafika kudzachita chifuniro chanu. Achotsa choyambacho, kuti akaike chachiwiricho. Ndi chifuniro chimenecho tayeretsedwa mwa chopereka cha thupi la Yesu Khristu, kamodzi, kwatha. Ndipotu wansembe aliyense amaima tsiku ndi tsiku, natumikira, napereka nsembe zomwezi kawirikawiri, zimene sizingathe konse kuchotsa machimo; koma Iye, (m’mene adapereka nsembe imodzi yamuyaya chifukwa cha machimo, anakhala padzanja lamanja la Mulungu(God);—NKJV) kuyambira pomwepo alindirira, kufikira adani ake aikidwa akhale mpando kumapazi ake. Pakuti ndi chipereko chimodzi anawayesera angwiro chikhalire iwo oyeretsedwa. Koma Mzimu Woyeranso atichitira umboni; pakuti adatha kunena, Ichi ndi chipangano ndidzapangana nao, atapita masiku ajawo, anena Ambuye: Ndidzapereka malamulo anga akhale pamtima pao; ndipo pa nzeru zao ndidzawalemba; ndipo machimo ao ndi kusaweruzika kwao sindidzakumbukiranso. Koma pomwe pali chikhululukiro (Kuchotsa) cha machimo palibenso chopereka cha kwa uchimo.” (Ahebri 10:9-18)  
Ndipo ife timakhulupilira kuti Yesu watipulumutsa ife ku machimo onse a dziko lapansi kudzera mu Ubatizo Wake ndi mwazi Wake pa Mtanda.
 
 
Chipulumutso cha Kubadwa Mwatsopano mwa Madzi ndi Mzimu Woyera chimene Chalembedwa M’mitima Mwathu ndi M’malingaliro athu
 
Kodi ndife olungama chifukwa chokha chakuti ife sitichimwanso?
Ayi. Ndife olungama chifukwa Yesu anachotsa machimo athu onse ndipo timakhulupirira mwa Iye.
 
Kodi inu nonse mumakhulupilira mu chipulumutso Wake changwiro? ―Amen.― Kodi inu mumamvera ndi Chikhulupiriro mau a God akuti Yesu Kristu Mwini anabatizidwa ndi kukhetsa mwazi pa Mtanda kuti atipulumutse ife? Ife tiyenera kumvera kuti tibadwe mwatsopano. Pamene ife takhulupilira kuti Yesu Kristu, kudzera mu uthenga wabwino wa kuchotsa uchimo, anatsuka machimo athu onse, komanso machimo onse a dziko lapansi, ife tingapulumutsidwe.
Ife sitingakhale angwiro pomvera Lamulo la God, koma ife tingakhale angwiro kudzera mu Chikhulupiriro chathu mu ntchito za Yesu Kristu. Yesu Kristu anatenga machimo athu onse kudzera mu ubatizo Wake mu Yordano ndi kulandira chiweruzo komanso chilango chifukwa cha machimo athu onse pa Mtanda. Pokhulupilira mu uthenga wabwino umenewu ndi mitima yathu yonse, ife tingaomboledwe ku machimo athu onse ndi kukhala olungama. Kodi inu mukukhulupilira zimenezi?
Ubatizo wa Yesu, kupachikidwa Wake ndi kuuka ndi za kufafaniza machimo onse a mtundu wa anthu, ndipo ndi lamulo la chipulumutso lokhazikika pa chikondi chopanda malire cha God. God amatikonda ife momwe ife tilili ndipo Iye ndi wolungama, choncho Iye anatipanga ife kukhala olungama choyamba. Yesu anatipanga ife kukhala olungama potenga machimo athu onse kudzera mu ubatizo Wake.
Kuti atsuke machimo athu onse, Iye anatuma Mwana Wake yekhayo, Yesu, ku dziko lino lapansi chifukwa cha ife. Iye analola Yesu kuti atenge machimo onse a dziko lapansi kudzera mu ubatizo wa Yesu ndipo kenako kupereka chiweruzo pa Mwana Wake cha machimo athu onse. Iye anatipanga ife kukhala ana olungama a God kudzera mu madzi ndi mwazi, ndiye chipulumutso chosatha ndi chopanda malire cha God.
Kwalembedwa mu Ahebri 10:16 kuti, “Ndidzapereka malamulo anga akhale pamtima pao; ndipo pa nzeru zao ndidzawalemba.”
M’mitima mwathu ndi m’maganizo mwathu, kodi ndife ochimwa pamaso pa God kapena kodi ndife olungama? Ngati ife tili ndi Chikhulupiriro m’Mau a God, ife timakhala olungama. Yesu Kristu anatenga machimo athu onse ndipo anaweruzidwa chifukwa cha iwo. Yesu Kristu ndi Mpulumutsi wathu. Ife tingaganize kuti, “Chifukwa chakuti ife timachimwa tsiku lililonse, kodi ife tingakhale bwanji olungama? Modziwikiratu ndife ochimwa.” Koma pamene ife tamvera mau a God monga Kristu Yesu anamvera Atate, ife timakhala olungama.
Kumene, monga momwe ndanenera m’mbuyomu, ife tidali ndi uchimo m’mitima mwathu ife tisanabadwe mwatsopano. Pambuyo poti tinalandira mu mitima mwathu uthenga wabwino wa kuchotsa machimo, ife tinapulumutsidwa ku machimo athu onse. Pamene ife sitinadziwe uthenga wabwino, ife tinali ochimwa. Koma ife tinakhala olungama pamene ife tinakhulupilira mu chipulumutso cha Yesu, ndipo kenako ife tinakhala ana olungama a God. Ichi ndi chikhulupiriro chokhala olungama chimene mtumwi Paulo analankhula. Chikhulupiriro mu uthenga wabwino wa kutsuka machimo chinatipanga ife kukhala ‘olungama’.
Osati mtumwi Paulo ngakhalenso Abrahamu ngakhalenso makolo a Chikhulupiriro anakhala olungama ndi ntchito zao, koma m’malo mwake pokhala ndi Chikhulupiriro ndi kumvera mau a God, mau a dalitso Wake.
Mu Ahebri 10:18, “Koma pomwe pali chikhululukiro (Kuchotsa) cha machimo palibenso chopereka cha kwa uchimo.” Monga kwalembedwera, God anatipulumutsa ife kuti tisafe chifukwa cha machimo athu. Kodi inu mukukhulupilira zimenezi? ―Amen.―
Mu Afilipi 2, “Mukhale nao mtima m’kati mwanu umene unalinso mwa Khristu Yesu, ameneyo, pokhala nao maonekedwe a Mulungu(God), sanachiyese cholanda kukhala wofana ndi Mulungu(God), koma anadzikhuthula yekha, natenga maonekedwe a kapolo, nakhala m’mafanizidwe a anthu; ndipo popezedwa m’maonekedwe ngati munthu, anadzichepetsa yekha, nakhala womvera kufikira imfa, ndiyo imfa ya pamtanda. Mwa ichinso Mulungu(God) anamkwezetsa Iye, nampatsa dzina limene liposa maina onse, kuti m’dzina la Yesu bondo lililonse lipinde, la za m’mwamba ndi za padziko, ndi za pansi padziko, ndi malilime onse avomere kuti Yesu Khristu ali Ambuye, kuchitira ulemu Mulungu(God) Atate.” (Afilipi 2:5-11)
Yesu Kristu sanapitirize chikhulupiriro m’dziko lapansi ndi mbiri yaikulu iliyonse ya Iye Mwini. M’malo mwake, Iye anatenga pa Iye Mwini maonekedwe a kapolo ndi kudza m’mafanizidwe a munthu. Iye anadzichepetsa Yekha ndi kukhala omvera kufikira imfa kuti atipulumutse ife.
Choncho, ife timatamanda Yesu, “Iye ndi God wathu, Mpulumutsi ndi Mfumu.” Chifukwa chimene timalemekeza God ndi kutamanda Yesu ndi chakuti Yesu anamvera Chifuniro cha Atate Wake mpaka kumapeto. Ngati Iye sakanamvera, ife sitikanalemekeza Mwana wa God tsopano. Koma chifukwa Mwana wa God anamvera chifuniro cha Atate Wake mpaka ku imfa, zolengedwa zonse ndi anthu onse pa dziko lapansi ili amamulemekeza Iye ndipo adzatero mpaka muyaya.
Yesu Kristu anakhala Mwanawankhosa wa God amene anatenga machimo a dziko lapansi, ndipo kwalembedwa kuti Iye anatenga iwo kudzera mu ubatizo Wake. Tsopano ndi pafupifupi zaka 2000 kuchokera pamene Iye anachotsa machimo a dziko lapansi. Ndipo chifukwa chakuti inu ndi ine takhala tikukhala m’dziko lino lapansi kuchokera pamene ife tinabadwa, machimo athu onse aphatikizidwanso m’machimo a dziko lapansi.
 
Kodi ife tidzakhala ochimwa ngati ife tachimwa mawa?
Ayi. Chifukwa Yesu anachotsa machimo athu onse a m’mbuyomu, a tsopano, ndi a m’tsogolo.
 
Popanda kusiyanitsa uchimo woyambirira ndi zolakwa zathu za moyo wathu wonse, kodi ife sitinachimwe kuchokera nthawi imene ife tinabadwa?
Yesu ankadziwa kuti ife tidzachimwa kuchokera tsiku limene ife tidzabadwa kufikira tsiku limene ife tidzafa ndipo Iye anachotsera machimo athu onse patsogolo. Kodi inu mukuona icho tsopano? Ngati tikanakhala ndi moyo mpaka zaka 70, machimo athu akanakwanira kudzaza magalimoto oposa zana otaya zinyalala. Koma Yesu anatenga uchimo onse kamodzi wa aliyense ndi ubatizo Wake, ndipo Iye anatenga chiweruzo cha machimo athu pa Mtanda.
Ngati Yesu akanachotsa kokha uchimo woyamba, tonse tikanafa ndi kupita ku gehena. Ngakhale tikanaganiza kuti Iye sakanatha kuchotsa machimo athu onse, sizingasinthe konse choonadi chakuti Yesu anafafaniza machimo athu onse.
Kodi ife tingachite machimo ochuluka bwanji m’dziko lino? Machimo onse amene ife timachita aphatikidwa m’machimo onse a dziko lapansi.
Pamene Yesu anauza Yohane kuti amubatize, ndi chimodzimodzi chimene Iye amatanthauza. Yesu anachitira umboni Iye mwini kuti anali atatenga machimo athu onse. God anatuma mtumiki Wake asanabwere Yesu ndipo anamupanga iye kuti abatize Yesu. Choncho, pobatizidwa ndi Yohane monga woimira mtundu wa anthu, powelamitsa mutu Wake pamaso pake kuti abatizidwe, Yesu anatenga machimo onse a anthu onse.
Machimo athu onse kuchokera zaka 20 kufika zaka 30, kuchokera zaka 30 kufika 40, ndi zina zotero; ngakhale machimo a ana athu anaphatikizidwa m’machimo a dziko lapansi, amene Yesu anatenga kudzera mu ubatizo Wake.
Kodi ndindani amene anganene kuti muli uchimo m’dziko lino lapansi? Yesu Kristu anatenga machimo onse a dziko lapansi. Ife tingapulumutsidwe tonse pamene ife takhulupilira m’mitima mwathu, popanda kukaikira ngakhale pang’ono, mu zomwe Yesu anachita kuti afafanizire machimo athu onse: Ubatizo Wake ndi kukhetsa kwa mwazi Wake wamtengo wapatali.
Anthu ambiri amakhala miyoyo yao yosokonezeka yokutiridwa m’maganizo mwao, kukamba za miyoyo yao ngati kuti miyoyo yao ndi zonse. Koma pali ambiri amene akhala miyoyo yovuta kwambiri. Anthu ambiri, kuphatikiza ine mwini, tinali ndi miyoyo yosokonezeka. Kodi inu simungamvetsetse bwanji kapena kuvomera uthenga wabwino wa kufafaniza machimo, wa ubatizo wa Yesu ndi mwazi Wake?
 
 
Chipulumutso cha Ochimwa Chakwaniritsidwa
 
Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu anasambitsa mapazi a Petro? 
Chifukwa chakuti Iye ankafuna kuti Petro akhale ndi Chikhulupiriro cholimba mu choona chakuti Iye adatsuka kale machimo ake onse a m’tsogolo kudzera mu ubatizo Wake. 
 
Tiyeni tiwerenge Yohane 19. “Ndipo anasenza mtanda yekha, natuluka kunka kumalo otchedwa Malo a Bade, amene atchedwa mu Chihebri, Gologota: kumene anampachika Iye; ndipo pamodzi ndi Iye awiri ena, chakuno ndi chauko, koma Yesu pakati. Koma Pilato analemba lembo, naliika pamtanda. Koma panalembedwa, YESU MNAZARAYO, MFUMU YA AYUDA. Ndipo lembo ilo analiwerenga ambiri a Ayuda; chifukwa malo amene Yesu anapachikidwapo anali pafupi pa mzindawo; ndipo linalembedwa mu Chihebri, ndi mu Chilatini, ndi mu Chigriki.” (Yohane 19:17-20)
Okondedwa anzanga, Yesu Kristu anatenga machimo onse a dziko lapansi ndipo Iye anagamulidwa kuti apachikidwe ku bwalo la Pilato. Tsopano tiyeni tiganizire za chochitika chimenechi pamodzi.
Kuchokera mu ndime 28 akuti, “Chitapita ichi Yesu, podziwa kuti zonse zidatha pomwepo kuti lembo likwaniridwe.” Yesu anatenga machimo athu onse kuti akwaniritse Lembo. Ndipo, Iye anena kuti, “Ndimva ludzu!”
“Kunaikidwako chotengera chodzala ndi vinyo wosasayo pa phesi la hisope, nachifikitsa kukamwa kwake. Pamene Yesu tsono adalandira vinyo wosasayo anati, Kwatha; ndipo anawerama mutu, napereka mzimu.” (Yohane 19:29-30) 
Ndipo patatha masiku atatu, Iye anaukitsidwa kwa akufa.
Ubatizo wa Yesu ndi Yohane Mbatizi ndi imfa Wake pa Mtanda zilumikizidwa mosathetseka, chimodzi chilibe chifukwa chopezeka popanda chinzake. Choncho, tiyeni titamande Ambuye Yesu chifukwa chotipulumutsa ife ndi Uthenga Wake Wabwino wa kuchotsa machimo.
Thupi la mtundu wa anthu nthawi zonse limatsata zofuna za thupi, ndipo ife sitingadzithandize koma kuchimwa ndi thupi lathu. Yesu Kristu anatipatsa ife ubatizo Wake ndi mwazi Wake kuti atipulumutse ife ku machimo a thupi lathu. Iye anatipulumutsa ife ku machimo a thupi lathu ndi uthenga Wake wabwino.
Iwo amene ali ndi kufafaniza konse kwa machimo ao angalowe ku ufumu wa kumwamba nthawi iliyonse pokhulupilira mwa Yesu, amene anabadwira m’Betelehemu, amene anabatizidwa mu Yordano, amene anafa pa Mtanda ndipo anaukitsidwa patatha masiku 3. Choncho ife timatamanda Ambuye ndi kulemekeza dzina Wake kwamuyaya.
M’mutu wotsiriza wa Yohane, Yesu anapita ku Galileya ataukitsidwa kwa akufa. Iye anapita kwa Petro ndi kunena kwa iye kuti, “Simoni mwana wa Yona, kodi undikonda Ine koposa awa?” ndipo Petro anamuyankha Iye ndi kunena kuti, “Inde, Ambuye; mudziwa kuti ndikukondani Inu.” Kenako Yesu anamuuza iye kuti, “Dyetsa anaankhosa anga.”
Petro anazindikira chilichonse, uthenga wabwino wa ubatizo wa Yesu ndi mwazi Wake, kufafaniza machimo. Tsopano kuti iye anakhulupilira mu uthenga wabwino wa madzi ndi mwazi zimene zinamupatsa iye kutsuka machimo, ndi kuzindikira chifukwa chimene Yesu anasambitsira mapazi ake, Chikhulupiriro chake mwa Yesu chinakhala cholimba kwambiri.
Tiyeni tiwerengenso Yohena 21:15. “Ndipo pamene atafisula Yesu ananena kwa Simoni Petro, Simoni mwana wa Yona, kodi undikonda Ine koposa awa? Ananena ndi Iye, Inde, Ambuye; mudziwa kuti ndikukondani Inu. Ananena naye, Dyetsa anaankhosa anga.” Iye anatha kupereka nkhosa Wake kwa Petro chifukwa chakuti Petro anali wophunzira Wake, chifukwa chakuti Petro adapulumutsidwa motheratu, komanso chifukwa chakuti Petro adakhala mtumiki olungama komanso wangwiro wa God.
Ngati Petro adakhala wochimwa chifukwa cha machimo ake a tsiku ndi tsiku, Yesu sakanamuuza iye kuti alalikire uthenga wabwino wa kuchotsedwa cha machimo, chifukwa chakuti iye, kuphatikiza ophunzira ena, sanadzithandize koma kuchimwa tsiku lililonse mthupi. Koma Yesu anauza iwo kuti alalikire uthenga wabwino umene unafafaniza machimo ao onse chifukwa chakuti iwo anakhulupilira mu ubatizo wa Yesu ndi mwazi Wake pa Mtanda, uthenga wabwino wa chitetezero cha machimo.
 
 
“Ambuye; Mudziwa Kuti Ndikukondani Inu”  
 
Kodi inu mudzakhalanso ‘ochimwa’ pamene inu mwachimwanso?
Ayi. Yesu anachotsera kale machimo anu onse a m’tsogolo ku Yordano.
 
Tiyeni tiganizire za mau a Yesu kwa Petro. “Simoni mwana wa Yona, kodi undikonda Ine koposa awa? Ananena ndi Iye, Inde, Ambuye; mudziwa kuti ndikukondani Inu.” Kuvomereza kwake kwa chikondi kunali koona, kutuluka monga kudachitira kuchokera mu chikhulupiriro mu uthenga wabwino wa chitetezero cha machimo onse.
Ngati Yesu sadaphunzitse Petro ndi ophunzira ena za uthenga wabwino wa kuchotsa machimo posambitsa mapazi ao, ndiye kuti iwo sakanatha kuvomereza chikondi chao munjira yotero.
Mmalo mwake, pamene Yesu anadza kwa iwo ndi kuwafunsa kuti, “Kodi undikonda Ine koposa awa?” Petro akananena kuti, Ambuye, ndine woperewera komanso ndine wochimwa. Ndine wochimwa amene sindingakukondeni Inu koposa awa. Chonde ndisiyeni ine.” Ndipo Petro akanathawa ndi kudzibisa yekha kwa Yesu.
Koma tiyeni tiganizire za mayankho a Petro. Iye anadalitsidwa ndi uthenga wabwino wa kufafaniza machimo, wa ubatizo wa Yesu ndi mwazi Wake umene unapulumutsa anthu onse.
Choncho, iye ananena kuti, “Inde, Ambuye; mudziwa kuti ndikukondani Inu.” Kuvomereza kwa chikondi kumeneku kunaturuka chifukwa cha Chikhulupiriro chake mu uthenga wabwino wa kutsuka machimo wa Yesu. Petro anakhulupilira mu uthenga wabwino woona wa kuchotsa machimo, umene Yesu anatengera machimo onse a dziko lapansi, ngakhale machimo a m’tsogolo amene anali omangidwa kuchita chifukwa cha kuperewera kwao komanso kufooka kwa thupi lao.
Chifukwa chakuti Petro anakhulupilira molimba mu uthenga wabwino wa kutsuka machimo, komanso chifukwa chakuti iye anakhulupiliranso kuti Yesu anali Mwanawankhosa wa God, iye anali othekera kuyankha Ambuye mosawiringula. Chipulumutso cha Yesu chinachokera ku uthenga wabwino wa kuchotsa machimo, ndipo motero Petro adapulumutsidwanso ku machimo ake onse a tsiku ndi tsiku. Petro adakhulupilira mu chipulumutso kudzera mu uthenga wabwino wa kufafaniza machimo onse a dziko lapansi.
Kodi inunso muli monga Petro? Kodi inu mungakonde ndi kukhulupilira mwa Yesu, amene anatenga machimo athu onse ndi uthenga Wake wabwino wa kuchotsa machimo, ndi ubatizo Wake ndi mwazi? Kodi inu simungakhulupilire bwanji mwa Iye ngakhalenso kumukonda Iye? Palibe njira ina.
Kukanakhala kuti Yesu adatenga kokha machimo a kale kapena a tsopano, ndi kusiya machimo a m’tsogolo kwa ife, ndiye kuti ife sitikanamutamanda Iye monga ife timachitira tsopano. Kuphatikiza ku zimenezi, ife tonse ndithudi tikanapita ku gahena. Choncho, ife tonse tiyenera kunena kuti ife tapulumutsidwa pokhulupilira mu uthenga wabwino wa kufafaniza machimo.
Thupi limakonda nthawi zonse kuchimwa, ndipo ife timachimwa nthawi zonse. Choncho, ife tiyenera kuvomereza kuti ife tapulumutsidwa pokhulupilira mu uthenga wabwino wa kuchuluka kwa kutsuka machimo umene Yesu watipatsa ife, ubatizo ndi mwazi wa Yesu.
Ngati ife sitinakhulupilire mu uthenga wabwino wa chitetezero cha machimo, umene ndi ubatizo ndi mwazi wa Yesu, palibe wokhulupilira amene adzapulumutsidwa ku machimo a moyo wao wonse. Kuowonjezera apo, ngati ife tinaomboledwa ku machimo a moyo wathu wonse povomereza ndi kulapa nthawi iliyonse, ife kwenikweni tikanakhala a ulesi kwambiri kukhala othera kukhala olungama nthawi zonse ndipo ife tikanakhala ndi uchimo m’mitima mwathu nthawi zonse.
Ngati ndi choncho, ife tikanapitiriza kubwerera m’mbuyo kukhala wochimwa ndipo sitikanatha kukonda Yesu kapena kuyandikira kwa Iye. Kenako ife sitikanatha kukhulupilira mu chipulumutso cha Yesu komanso ife sitikanatha kutsata Iye mpaka kumapeto a miyoyo yathu.
Komabe, Yesu anatipatsa ife uthenga wabwino wa kufafaniza machimo ndi kupulumutsa iwo amene anakhulupilira. Iye wakhala Mpulumutsi wangwiro ndi kutsuka zolakwa zonse zimene ife timachita tsiku lililonse m’miyoyo yathu kuti ife timukondedi Iye.
Choncho, ife okhulupilira sitingadzithandize koma kukonda uthenga wabwino wa ubatizo ndi mwazi wa Yesu, wa kutsuka machimo athu. Okhulupilira onse angakonde Yesu kwamuyaya ndi kukhala akapolo a chikondi cha chipulumutso kudzera mu kuchotsa machimo chimene Yesu watipatsa ife.
Wokondedwa kwambiri. Ngati Yesu akadasiya ngakhale uchimo wochepa mmbuyo, ndiye kuti inu simukanatha kukhulupilira mwa Yesu, ngakhalenso inu kutha kukhala mboni ya uthenga wabwino wa kutsuka machimo. Inu simukanatha kugwira ntchito monga mtumiki wa God.
Koma ngati inu mumakhulupilira mu uthenga wabwino wa kufafaniza machimo, inu mungapulumutsidwe ku machimo onse a dziko lapansi. Iye amalola inu kupulumutsidwa ku machimo onse a dziko lapansi pamene inu mwazindikira uthenga wabwino woona wa kutsuka machimo wolembedwa m’mau a Yesu.
 
 
“Kodi Undikonda Ine Koposa Awa?” 
 
Kodi ndi chiyani chatipanga ife kukonda Yesu kuposa china chilichonse?
Chikondi Wake pa ife kudzera mu ubatizo Wake umene unatsuka machimo athu onse, ngakhale machimo athu onse a m’tsogolo 
 
God anapereka nkhosa Wake kwa atumiki Wake, amene anakhulupilira motheratu mu uthenga wabwino wa kutsuka machimo. Yesu anafunsa katatu kuti, “Simoni mwana wa Yona, kodi undikonda Ine koposa awa?” ndipo Petro ankayankha nthawi iliyonse kuti, “Inde, Ambuye; mudziwa kuti ndikukondani Inu.” Tsopano, tiyeni tiganizire za mayankho a Petro. Ife tingaone kuti ichi si chionetsero cha chifuniro chake, koma Chikhulupiriro chake mu uthenga wabwino wa kuchotsa machimo.
Pamene ife takonda winawake, ndipo ngati chikondi chimenecho ndi chobwadwa chifukwa cha chifuniro chathu, icho chingazilale pamene ife tafooka. Koma ngati chikondi chimenecho chatengera pa mphamvu ya chikondi Chake, ndiye kuti icho chingakhale kwa muyaya. Chikondi cha God, chotchedwa, chitetezero chochuluka cha machimo athu onse, chipulumutso cha madzi a ubatizo wa Yesu ndi Mzimu Woyera, chili monga choncho.  
Chikhulupiriro chathu mu uthenga wabwino wa kuchotsa machimo, chiyenera kutumikira monga maziko a chikondi cha Ambuye kwa ife. Ngati ife tinamukonda Iye ndi chifuniro chathu chokha monga maziko athu, ife tidzapunthwa mawa ndi kudzida tokha chifukwa cha mphulupulu zathu pamapeto pake. Komabe, Yesu anatsuka machimo athu onse: uchimo woyambilira, machimo athu a tsiku ndi tsiku a kale, machimo a mawa, komanso machimo onse a moyo wathu wonse. Iye sanapatule winawake pa dziko lonse la pansi ku chipulumutso Wake.
Zonse zimenezi ndi zoona. Ngati chikondi chathu ndi chikhulupiriro chathu zikadalira pa chifuniro chathu, ife tikanalephera mu chikhulupiriro chathu. Koma chikondi chathu ndi chikhulupiriro chathu chimadalira pa uthenga wabwino wa kutsuka machimo umene Yesu watipatsa ife, ndife kale ana a God, olungama. Chifukwa chakuti ife timakhulupilira mu chipulumutso cha madzi ndi Mzimu Woyera, ndife opanda uchimo.
Popeza chipulumutso chathu chinadza, osati kuchokera ku Chikhulupiriro chathu mwa ife eni koma kuchokera ku chikondi cha God, lamulo Wake la chipulumutso choona kudzera mu kutsuka machimo, ndife olungama zilibe kanthu momwe ife tingakhalire operewera kapena ofooka m’moyo weniweni. Ife tidzapita ku ufumu wa kumwamba ndipo pamapeto pake tidzatamanda God kwamuyaya. Kodi inu mukukhulupilira zimenezi?
1 Yohane 4:10 ikunena kuti, “Umo muli chikondi, sikuti ife tinakonda Mulungu(God), koma kuti Iye anatikonda ife, ndipo anatuma Mwana wake akhale chiombolo chifukwa cha machimo athu.” Yesu anatipulumutsa ife ndi madzi ndi Mzimu Woyera, choncho ife tiyenera kukhala ndi Chikhulupiriro mu uthenga wabwino wa kuchotsa machimo, ubatizo wa Yesu ndi mwazi Wake. 
Kukanakhala kuti God sadatipulumutse ife ndi uthenga wabwino wa kuchotsa machimo, ndiye kuti ife sitikanapulumutsidwa, ngakhale ife tikadakhulupilira motani. Koma Yesu anatsuka machimo onse amene timachita m’mitima mwathu ndi thupi lathu.
Kwa ife kuti tikhulupilire mwa God, kuti tikhale olungama, ife tiyenera kukhala otsimikiza za chipulumutso chathu kudzera mu Chikhulupiriro m’mau a madzi ndi Mzimu Woyera, uthenga wabwino wa kufafaniza machimo. Uthenga wabwino wa kuchotsa machimo onse a dziko lapansi ndi kukhala ndi Chikhulupiriro mu ubatizo wa Yesu ndi mwazi Wake. Uthenga wabwino wa kutsuka machimo ndi Chikhulupiriro choona, maziko enieni a chipulumutso, mfungulo ku uthenga wabwino wa God.
 
 
Ife Tiyenera Kutaya Chikhulupiriro cha Chifuniro Chathu 
 
Kodi Chikhulupiriro choona chimachokera kuti?
Icho chimachokera ku chikondi cha Ambuye, amene watsuka kale machimo athu onse a tsopano ndi a m’tsogolo.  
 
Chikhulupiriro kapena chikondi chobadwa kuchokera ku chifuniro cha munthu sichili chikondi choona kapena chikhulupiriro choona. Alipo ambiri m’dziko lino amene poyamba amakhulupirira Yesu ndi chifuniro chabwino, kenako amasiya chikhulupiriro chawo kwathunthu chifukwa cha tchimo m’mitima yawo.
Koma ife tiyenera kudziwa kuti Yesu anatsuka machimo onse a dziko lapansi: osati mphulupulu zazing’ono chabe, koma machimonso aakulu amene amachitidwa kudzera mu umbuli.
Ndipo mu Yohane 13, kuti aphunzitse ophunzira Wake momwe chipulumutso Wake chinali chokwanira zonse, Yesu anasonkhanitsa pamodzi ophunzira Wake Iye asanapachikidwe. Panthawi ya chakudya Wake ndi ophunzira, Iye ananyamuka ndi kutsuka mapazi awo kuti aonetse choonadi cha chipulumutso Wake. Ife tiyenera tonse kudziwa ndi kukhulupilira mu uthenga wabwino wa kutsuka machimo, umene Yesu anaphunzitsa ophunzira powasambitsa mapazi ao.
Koma Petro motsimikiza anakana kulola Yesu kuti asambitse mapazi ake poyamba. “Simudzasambitsa mapazi anga kunthawi yonse.” Ndipo ichi chinali chionetsero cha chikhulupiriro chobadwa kuchokera ku chifuniro chake. Koma Yesu anamuuza iye kuti, “Chimene ndichita Ine suchidziwa tsopano; koma udzadziwa m’tsogolo mwake.”
Tsopano, ndi uthenga wabwino wa madzi ndi Mzimu Woyera, ife tingamvetsetse mau a Yesu. Iwo ndi mau a choonadi, uthenga wabwino wa madzi ndi Mzimu Woyera, kuchotsa machimo, umene umalola ochimwa kukhala olungama pokhulupilira ndi mtima wake wonse.
Petro anapita kokawedza nsomba ndi ophunzira. Iwo ankawedza nsomba monga momwe ankachitira iwo asanakumane ndi Yesu. Kenako Yesu anaonekera kwa iwo ndi kuwaitana iwo. Yesu adawakonzera chakudya cha m’mawa, petro anazindikira tanthauzo la mau amene Yesu adalankhula poyamba. “Chimene ndichita Ine suchidziwa tsopano; koma udzadziwa m’tsogolo mwake.” Iye pamapeto pake adazindikira zimene kwenikweni Yesu anatanthauza posambitsa mapazi ake poyamba.
“Ambuye anatsuka machimo anga onse. Machimo onse amene ndimachita chifukwa cha zofooka zanga, kuphatikiza machimo onse amene ndidzachitanso m’tsogolo.” Choncho Petro anasiya Chikhulupiriro chobadwa mwa chifuniro chake ndi kuyamba kukhulupilira mu ubatizo ndi mwazi wa Yesu, uthenga wabwino wa kutsuka uchimo.
Atatsiriza kudya chakudya cha m’mawa, Yesu anafunsa Petro kuti, “kodi undikonda Ine koposa awa?” Tsopano, polimba ndi Chikhulupiriro mu chikondi cha Yesu, Petro anavomereza. “Inde, Ambuye; mudziwa kuti ndikukondani Inu.” Petro ananena icho chifukwa chakuti iye adazindikira zimene Yesu adatanthauza pamene Iye ananena kuti, “koma udzadziwa m’tsogolo mwake.” Iye anatha kuvomereza chikhulupiriro chake choona, chikhulupiriro mu ubatizo ndi mwazi wa Yesu, uthenga wabwino wa kufafaniza machimo.
 
 
Pambuyo Pake, Iye Anakhala Mtumiki Weniweni wa God 
 
Choncho, pambuyo pa zimenezo, Petro ndi ophunzira ena analalikira uthenga wabwino kufikira mapeto a masiku ao. Ngakhale Paulo, amene adalondalonda Akristu mopanda chisoni, anachitira umboni ku uthenga wabwino m’masiku ovuta amenewo a Ufumu wa Chiroma.
 
Kodi inu mungakhale bwanji mtumiki weniweni wa God?
Pokhulupilira mu chitetezero Chake cha muyaya cha machimo anga onse 
 
Mwa ophunzira khumi ndi awiri a Yesu, Yudasi anagulitsa Yesu ndi kudzikhweza yekha pambuyo pake. Ndipo anali mtumwi Paulo amene anatenga malo ake. Ophunzira adasankha Matiyasi pakati pawo, koma anali Paulo amene God anasankha, choncho Paulo anakhala mtumwi wa Yesu ndi kulalikira uthenga wabwino wa kuchotsa machimo ndi ophunzira onse a Yesu.
Ambiri a ophunzira a Yesu anafa monga ofera Chikhulupiriro. Ngakhale pamene anaopsezedwa ndi imfa, iwo anapitiriza kulalikira uthenga wabwino woyambirira. 
“Yesu Kristu anatsuka machimo onse a thupi lanu ndi uthenga Wake wabwino wa ubatizo ndi mwazi, ndiye kuti, ndi uthenga Wake wabwino wa kuchotsa machimo. Yesu anatenga machimo anu ndi ubatizo Wake mu Yordano ndi kutenga chiweruzo cha inu pa Mtanda. Khulupilirani mu uthenga wabwino wa ubatizo wa Yesu ndi mwazi Wake pa Mtanda, ndi kupulumutsidwa.”
Ambiri indedi anapulumutsidwa pokumva uthenga wabwino ndi kukhulupilira mu uwo. Inali mphamvu ya Chikhulupiriro mu uthenga wabwino wa ubatizo wa Yesu, mwazi Wake, ndi Mzimu Woyera.
Ophunzira analalikira uthenga wabwino wa madzi ndi Mzimu Woyera kuti, “Yesu ndi God komanso Mpulumutsi.” Ndi chifukwa chakuti iwo achitira umboni za uthenga wabwino wa madzi ndi Mzimu Woyera, kuti inu ndi ine tsopano tingamve uthenga wabwino wa ubatizo ndi mwazi wa Yesu, wa chipulumutso, ndi kupulumutsidwa ku uchimo. Chifukwa cha chikondi chopanda malire cha God komanso chopulumutso chathunthu cha Yesu, ife tonse takhala ophunzira a Yesu.
Kodi inu nonse mukukhulupilira? Yesu anatikonda ife kwambiri kuti Iye anatipatsa ife uthenga wabwino wa madzi ndi Mzimu Woyera, kuchotsa uchimo, ndipo ife takhala ophunzira olungama a Yesu. Kuti aphunzitse uthenga wabwino woona wa kutsuka machimo, Yesu anasambitsa mapazi a ophunzira Wake.
Yesu anasambitsa mapazi a ophunzira Wake kuti awaphunzitse iwo ndi ife kuti machimo onse a dziko lapansi, machimo onse amene ife timachita m’miyoyo yathu yonse, anatsukidwa motheratu pamene Yesu anabatizidwa ndi kukhetsa mwazi pa Mtanda. Ndipo ife tikuthokoza God chifukwa cha chikondi Wake ndi uthenga wabwino wa kuchotsa machimo.
Yesu anatiphunzitsa ife zinthu ziwiri posambitsa mapazi a ophunzira. Choyamba, kunali kuphunzitsa iwo, monga momwe iye adanenera kuti, “Chimene ndichita Ine suchidziwa tsopano; koma udzadziwa m’tsogolo mwake.” Kuti machimo athu onse anatsukidwa ndi uthenga wabwino wa kufafaniza machimo, ubatizo wa Yesu ndi mwazi Wake.
Chiphunzitso chachiwiri chinali chakuti monga Yesu anadzichepetsa Yekha kuti apulumutse ochimwa ndi kuwapanga iwo kukhala olungama, ife, obadwanso mwatsopano, tiyenera kutumikira ena polalikira uthenga wabwino wa kutsuka machimo. Ndi zolondola kwa ife amene tinabwera poyamba, kutumikira iwo amene akubwera pambuyo.
Zifukwa ziwiri zimene Yesu anasambitsa mapazi a ophunzira Ake tsiku limodzi lisanafike phwando la Paska ndi zomveka bwino, ndipo izo zidakalipo mkati mwa Mpingo.
Ophunzira sangakhale wapamwamba kuposa mphunzitsi wake. Choncho, ife timalalikira uthenga wabwino ku dziko lapansi ndi kutumikira uwo monga ngati tikutumikira Yesu. Ndipo ife, amene tinapulumutsidwa poyamba, tiyenera kutumikira iwo amene abwera pambuyo pa ife. Kuti aphunzitse zimenezi, Yesu anasambitsa mapazi a ophunzira. Kuonjezera apo, posambitsa mapazi a Petro, Iye anationetsa ife kuti Iye ndi Mpulumutsi wangwiro wa ife kuti ife tisanyengedwenso ndi mdierekezi.
Inu nonse mungapulumutsidwe pokhulupilira mu uthenga wabwino wa kuchotsa machimo, wa madzi ndi Mzimu Woyera. Yesu anatsuka machimo athu onse ndi ubatizo Wake, kupachikidwa, ndi kuukitsidwa, ndipo okhawo amene amakhulupilira mu uthenga Wake wabwino angapulumutsidwe ku machimo a dziko lapansi kwamuyaya.
 
 
Kukhala ndi Chikhulupiriro mu Uthenga Wabwino Umene Unatsuka Machimo Athu Onse a Tsiku ndi Tsiku
 
Ife tingadule chinyengo cha mdierekezi pokhulupilira mu uthenga wabwino wa kufafaniza machimo, mau a madzi ndi Mzimu Woyera. Anthu amanyengedwa mosavuta ndi mdierekezi ndipo mdierekezi amanong’ona mmakutu mwathu mopitilira. Podziwa kuti thupi la anthu limachimwa m’dziko lapansi, kodi iwo angakhale bwanji opanda uchimo? Anthu onse ndi ochimwa.
Ife tikudziwa yankho. “Podziwa kuti Yesu anachotsa machimo onse a thupi lathu ndi ubatizo Wake, kodi wokhulupirira angakhale bwanji ndi uchimo? Yesu analipira kwathunthu malipiro onse a uchimo, ndipo ndi uchimo lanji lomwe latsala kuti ife tilipire?”
Ngati sitimakhulupirira uthenga wabwino wa madzi ndi mwazi, mawu a mdierekezi amawoneka ngati oyenera. Koma, ngati tili ndi uthenga wabwino kumbali yathu, tikhoza kukhala ndi chikhulupiriro chosagwedezeka mu choonadi cha mawu a God.
Choncho ife tiyenera kukhala ndi Chikhulupiriro mu uthenga wabwino wa kubadwa mwatsopano mwa madzi ndi mwazi. Chikhulupiriro choona ndi kukhulupilira mu uthenga wabwino wa Ubatizo wa Yesu, mwazi Wake pa Mtanda, imfa Wake ndi kuuka Wake. 
Kodi munayamba mwawonapo chithunzi cha chitsanzo cha chihema chopatulika? Ndi nyumba yaing’ono. Nyumbayo ndi yogawidwa m’magawo awiri, gawo la kunja ndi malo opatulika ndipo gawo la mkati ndi malo opatulika kwambiri amene ali ndi chotetezerapo.
Pali zipilala zonse 60 zoimirira m’Bwalo la kunja la Chihema, ndipo malo opatulika ali ndi matabwa 48. Ife tiyenera kukhala ndi chithunzi cha chihema chopatulika mmaganizo mwathu kuti timvetsetse tanthauzo la mau a God.
 
 
Kodi Chipata cha Bwalo la Chihema Chinapangidwa ndi Chiyani?
 
Kodi chipata cha bwalo la Chihema chinapangidwa ndi chiyani?
Nsaru ya lamadzi, lofiirira, ndi lofiira, ndi bafuta wa thonje losansitsa.
 
Chipata cha bwalo la Chihema chafotokozedwa mu Eksodo 27:16 kuti, “Ndipo pa chipata cha bwalolo pakhale nsalu yotsekera ya mikono makumi awiri, ya lamadzi ndi lofiirira, ndi lofiira, ndi bafuta wa thonje losansitsa, ntchito ya wopikula; nsichi zake zikhale zinai, ndi makamwa ao anai.” Zipangizo zogwiritsa ntchito pa chipata cha bwalo la Chihema zinali thonje la lamadzi, ndi lofiirira, ndi lofiira, ndi bafuta wa thonje losansitsa. Inali yolukidwa mwaluso ndi yosiyana maonekedwe kwambiri.
God analamula Mose kuluka chipata mwamitundu ndi thonje la lamadzi, lofiirira, ndi lofiira kuti chikhale chosavuta kwa aliyense kupeza cholowera. Ndipo chipatacho cholukidwa ndi thonje la lamadzi, lofiirira, lofiira, ndi bafuta wa thonje losansitsa chinapachikidwa pa mizati inayi.
Zipangizo zinayi izi zikufanizira dongosolo la chipulumutso cha God, limene kudzera mwa ilo Iye akanapulumutsa onse amene anakhulupirira mwa Mwana Wake, mu ubatizo ndi mwazi wa Yesu, ndi mu kukhala Kwake God.
Chipangizo chilichonse chogwiritsidwa ntchito kumanga chihema chopatulika chili ndi tanthauzo lapadera ndipo icho chimaimira mau a God komanso dongosolo Wake kuti apulumutse mtundu wa anthu kudzera mwa Yesu.
Tsopano, kodi zinagwiritsidwa ntchito zipangizo zingati zosiyana pa chipata cha bwalo la chihema chopatulika? Thonje lamadzi, lofiirira, lofiira, ndi bafuta wa thonje losansitsa. Ndipo zinayi izi ndi zofunika kwambiri potithandiza kulimbitsa chikhulupiriro chathu mu uthenga wabwino wa kubadwa mwatsopano. Ngati sizikanakhala zofunika, nkhaniyi sibwenye inalembedwa m’Baibulo mwatsatanetsatane chonchi.
Popeza zipangizo zonse zogwiritsidwa ntchito pa chipata cha bwalo la Chihema ndi Chihema zinali gawo lofunika la chipulumutso, zinayenera kupangidwa ndi thonje lamadzi, lofiirira, lofiira, ndi bafuta wa thonje losansitsa. Chipulumutso chimenechi chinatsuka machimo athu onse a tsiku ndi tsiku, machimo oyambilira, komanso machimo a m’tsogolo. Choncho, God anavumbulutsa zinthu zimenezi kwa Mose ndi kumuuza iye kuti achite ndendende monga momwe iye anauzidwira.
 
 
Kodi Thonje Lamadzi, Lofiirira, ndi Lofiira Zimatanthauza Chiyani mkati mwa Uthenga Wabwino wa God?
 
Kodi zipangizo zonse zogwiritsidwa ntchito pa chihema zinkaimira chiyani?
Chipulumutso cha Yesu kudzera mu ubatizo Wake ndi mwazi Wake
 
Mkati mwa chihema chopatulika, thonje lamadzi, lofiirira, ndi lofiira, ndi bafuta wa thonje losansitsa zinagwiritsidwanso ntchito pa nsalu yotchinga yopachikidwa pakati pa malo opatulika ndi malo opatulika kwambiri. Zipangizo zomwezo zinagwiritsidwa ntchito pa mikanjo ya mkulu wansembe, amene anatumikira mkati mwa chihema chopatulika.
Thonje lamadzi limaimira ubatizo wa Yesu. Mu 1 Petro 3:21, kunanenedwa kuti, “Chimenenso chifaniziro chake chikupulumutsani tsopano, ndicho ubatizo.” Ubatizo wa Yesu umene Iye anatengera machimo onse a dziko lapansi unatsimikiziridwa ndi Petro mu ndime imeneyi, monga chifaniziro cha chipulumutso cha chitetezero. Machimo anthu onse, machimo onse a dziko lapansi, anaperekedwa pa Yesu pa ubatizo Wake. Choncho, thonje lamadzi, ubatizo wa Yesu, ndi gawo lofunika kwambiri la mau a chipulumutso.
Thonje lofiira limaimira mwazi wa Yesu, ndipo thonje lofiirira limaimira ufumu―udindo wa Yesu monga Mfumu ndi God. Choncho, mitundu itatu ya thonje inali yofunika ku chikhulupiriro chathu mwa Yesu ndi chipulumutso Wake. 
Chovala chokongola chimene mkulu wa ansembe anavala chinatchedwa efodi, ndipo mwinjiro wa efodi unali lamadzi lonse. Mkulu Wansembe ankavala nduwira m’mutu mwake imene mbale ya golidi waphanthiphanthi woona inali kulochedwa ndi chosindikizira, ‘KUPATULIKIRA YEHOVA’. Ndipo mbaleyi imakiidwa pamkuzi wamadzi panduwira.
 
 
Choonadi Choimiriridwa ndi Thonje Lamadzi
 
Kodi thonje lamadzi limaimira chiyani?
Ubatizo wa Yesu
 
Ndinafufuza tanthauzo la thonje lamadzi m’Baibulo. Kodi Baibulo limanena chiyani za lamadzi? Tiyenera kumvetsetsa thonje lamadzi pakati pa thonje lamadzi, lofiirira, ndi lofiira.
Thonje lamadzi limatanthauza ubatizo wa Yesu. Yesu Kristu anabatizidwa ndi Yohane Mbatizi kuti atenge machimo onse a dziko lapansi (Mateyu 3:15).
Akanakhala kuti Yesu sanatenge machimo onse a dziko lapansi ndi ubatizo Wake, ndiye kuti ife sitikanakhala oyeretsedwa pamaso pa God. Choncho, Yesu Kristu adadza ku dziko lino lapansi ndi kubatizidwa ndi Yohane Mbatizi mu Mtsinje wa Yordano kuti atenge machimo onse a dziko lapansi.  
Chifukwa chimene panayenera kukhala thonje lamadzi pa chipata cha bwalo la chihema chopatulika chinali chakuti sitikanakhala oyeretsedwa popanda ubatizo wa Yesu.
Thonje lofiira limatanthauza imfa ya Yesu. Lofiirira limatanthauza Mzimu Woyera, kotero udindo wa Yesu monga “Mwini Mphamvu yekha, Mfumu ya mafumu ndi Mbuye wa ambuye.” (1 Timoteo 6:15)
Thonje lofiira limatanthauza mwazi wa Kristu, amene anakhetsa pa Mtanda kuti alipire mphotho ya uchimo ya mtundu wonse wa anthu. Yesu Kristu anadza ku dziko lino lapansi m’thupi kuti atenge machimo onse a mtundu wa anthu pa Iye Mwini kudzera mu Ubatizo Wake, asanadzipereke Yekha nsembe pa Mtanda kuti akwaniritse kuchotsa uchimo. Ubatizo wa Yesu ndi uthenga wabwino woona wa kutsuka machimo, umene unaneneredwa kudzera m’mitundu ya thonje yogwiritsidwa ntchito ku chihema chopatulika cha m’Chipangano Chakale.
Nsichi za chihema zinapangidwa ndi mtengo wakasiya, ndipo makamwa ake anali amkuwa, ndipo makamwa amkuwa anakutidwa ndi mibande yasiliva.
Ochimwa onse adayenera kuweruzidwa chifukwa cha machimo ao chifukwa chakuti mphotho ya uchimo ndi imfa. Winawake asanadalitsidwe ndi God kuti abadwe mwatsopano, iye ayenera kuzindikira kuti iye ayenera kuweruzidwa chifukwa cha machimo ake.
Choncho, ubatizo wa Yesu wa m’Chipangano Chatsopano, umene umaimiriridwa ndi thonje lamadzi la chihema chopatulika cha m’Chipangano Chakale, unatenga machimo athu onse. Yesu anatenga machimo athu kupita nao pa Mtanda kuti akhetse mwazi ndipo anaweruzidwa chifukwa cha iwo. Pochita choncho, Iye anapulumutsa tonse a ife amene tili ndi Chikhulupiriro mu uthenga wabwino wa kutsuka machimo. Iye ndi Mfumu ya mafumu komanso God Woyera.
Okondedwa, ubatizo wa Yesu unali chipulumutso cha Yesu, amene anatipulumutsa ife potenga machimo athu onse. Yesu, amene ndi God, anadza ku dziko lapansi m’thupi; Iye anabatizidwa kuti atenge machimo onse a dziko lapansi; Iye anapachikidwa ndi kukhetsa mwazi pa Mtanda kuti alandire chiweruzo m’malo mwathu. Ubatizo wa Yesu umatiuza ife mosakaikira kulikonse kuti Iye adakhala Mpulumutsi woona wa mtundu wonse wa anthu.
Ife tingaonenso icho mu mitundu imene inagwiritsidwa ntchito ku chipata cha chihema chopatulika. Kugwiritsa ntchito kwa bafuta wa thonje losansitsa kumatanthauza kuti Iye anapulumutsa tonse a ife mosachotsera ku machimo onse a dziko lapansi.
Kusoka nsalu ya chipata ndi thonje lamadzi, lofiirira, ndi lofiira mu ulusi wa bafuta kunali kutiuza ife momveka bwino choonadi cha chipulumutso cha God. Ichi chinali chofunika kwambiri ku chipulumutso cha chitetezero.
Ife tingaone kuchokera ku zipangizo zogwiritsidwa ntchito ku chipata cha chihema chopatulika kuti Yesu Kristu sanatipulumutse ife ochimwa mwachisawawa, popanda kukonzekera. Iye, potsatira dongosolo latsatanetsatane la God mosamala, anabatizidwa ndi kupachikidwa, kenako anauka kwa akufa kuti akwaniritse chipulumutso cha mtundu wa anthu. Ndi thonje lamadzi, lofiirira, ndi lofiira, zipangizo za uthenga wabwino wa kutsuka machimo, Yesu anapulumutsa onse amene anakhulupirira chipulumutso Wake.
 
 
Mkhate wa Mkuwa wa m’Chipangano Chakale Unali Chithunzi-thunzi cha Ubatizo wa m’Chipangano Chatsopano
 
Kodi ndi chifukwa chiyani ansembe ankasamba manja ao ndi mapazi iwo asanalowe m’malo opatulika?
Chifukwa chakuti iwo ankayenera kuimilira pamaso pa God popanda tchimo lililonse.
 
Mkhate unapangidwanso ndi mkuwa. Mkuwa umaimira chiweruzo chimene Yesu anavutikira chifukwa cha ife. Mbiya ya madzi imaimira mau a uthenga wabwino, amene amatiuza ife kuti mphulupulu zathu zonse zinatsukidwa.
Izo zimationetsa ife momwe kutsuka kwa machimo athu kunachitikira. Ndi mthunzi wa choonadi chakuti machimo onse a dziko lapansi angatsukidwe kudzera mu chikhulupiriro m’mau a ubatizo wa Yesu.
Guwa la nsembe yopsereza limaimilira chiweruzo. Ndipo madzi a Yesu, amene ndi mtundu wamadzi, ndi uthenga wabwino wa chitetezero cha machimo, ubatizo wa Yesu kudzera mwa Yohane Mbatizi (Mateyu 3:15, 1 Yohane 5:5-10). Ndi mau a umboni wa uthenga wabwino wa chipulumutso kudzera mu chitetezero.
Mu 1 Yohane 5, kwalembedwa kuti, “Ndipo ichi ndi chigonjetso tichigonjetsa nacho dziko lapansi, ndicho chikhulupiriro chathu. Pakuti pali atatu akuchita umboni, Mzimu Woyera, ndi madzi, ndi mwazi; ndipo iwo atatu ali mmodzi.” Iye akutiuzanso ife kuti iye amene amakhulupilira mwa Mwana wa God ali ndi umboni wa madzi, mwazi, ndi Mzimu Woyera mwa iye.
God anatilola ife kuti tiyeretsedwe kudzera mu Chikhulupiriro mu uthenga wabwino wa chitetezero ndi kulowa mu chihema chopatulika. Choncho, ife tsopano tingakhale mu Chikhulupiriro, kudyetsedwa mau a God, kudalitsidwa ndi Iye, ndi kukhala moyo wa olungama. Kukhala anthu a God kumatanthauza kupulumutsidwa kudzera mu Chikhulupiriro mu uthenga wabwino wa chitetezero ndi kukhala mkati mwa chihema chopatulika.
Anthu ambiri lero amati nkokwanira kungokhulupirira popanda kuganizira tanthauzo la thonje lamadzi, lofiirira, ndi lofiira la pa chipata cha chihema chopatulika. Ngati wina anakhulupilira mwa Yesu popanda kudziwa za zinthu zimenezi, Chikhulupiriro chawo si choona chifukwa chakuti mudakali uchimo m’mitima mwao. Anthu angakhalebe ndi uchimo m’mitima mwao chifukwa chakuti iwo sakhulupilira mu choonadi cha kubadwa mwatsopano kudzera mu uthenga wabwino wa chitetezero, wa madzi, mwazi, ndi Mzimu Woyera.
Ngati winawake wapemphedwa kuti afotokoze za munthu amene sakumudziwa nkomwe, ndipo ngati, pofuna kukondweretsa womverayo, iye wanena kuti, “Inde, ndimakhulupilira munthu ameneyu. Sindidakumanepo naye, koma ndimamukhulupilirabe iye.” Kodi inu mukuganiza kuti womverayo adzakondwera kumva icho? Mwina ena a inu mungakondwere, koma ichi si Chikhulupiriro chimene God amafuna kuchokera kwa ife.
God amafuna ife kukhulupilira mu uthenga wabwino wa kuchotsa machimo, chipulumutso cha Yesu kudzera mtundu wamadzi (ubatizo), wofiirira (ufumu), ndi wofiira (mwazi). Ife tiyenera kudziwa, tisanakhale ndi Chikhulupiriro mwa Yesu, momwe Iye anatipulumutsira ife ku uchimo onse.
Pamene ife takhulupilira mwa Yesu, ife tiyenera kudziwa momwe Iye anatipulumutsira ku machimo athu onse kudzera m’madzi (ubatizo wa Yesu), mwazi (imfa Wake), ndi Mzimu Woyera (Yesu kukhala God).
Pamene ife tamvetsetsadi, ife tingakumane ndi Chikhulupiriro choona ndi kukhala ndi Chikhulupiriro chathunthu. Chikhulupiriro chathu sichingakhale konse chathunthu popanda kudziwa choonadi chimenechi. Chikhulupiriro choona chimadza kokha pomvetsetsa umboni wa chipulumutso cha Yesu, uthenga wabwino wa kuchotsa machimo, ndi Yesu kukhala Mpulumutsi woona wa mtundu wa anthu.
Kodi, nanga, Chikhulupiriro chimene chimanyoza Yesu ndi chotani? Tiyeni tione.
 
 
Chikhulupiriro Chimene Chimanyoza Yesu
 
Kodi chofunika kwambiri pa Chikhulupiriro ndi chiyani?
Chidziwitso chenicheni cha ubatizo wa Yesu 
 
Inu muyenera kudziwa kuti kukhulupirira mwa Yesu mwachisawawa ndi kumunyoza Iye. Ngati inu mukuganiza kuti, “Ndimachiona kukhala chovuta kukhulupilira, koma monga Iye ali God komanso monga Iye ali Mwana wa God, ndiyenera kukhulupilira,” ndiye kuti inu mukunyoza Yesu. Inu muyenera kukhulupilira mu ubatizo ndi mwazi wa Yesu, uthenga wabwino wa chitetezero.
Kukhulupilira mwa Yesu popanda kudziwa uthenga wabwino wa kufafaniza machimo ndi koipa kwambiri kuposa kusakhulupilira mwa Yesu konse. Kulalikira uthenga wabwino umene umakhulupilira kokha m’mwazi wa Yesu ndi kugwira ntchito pachabe popanda kudziwa choonadi.
Yesu safuna aliyense kumukhulupirira Iye mwachisankho, kapena popanda chifukwa. Iye amafuna ife kukhulupilira mwa Iye kudzera mu kudziwa uthenga wabwino wa chitetezero.
Pamene ife takhulupilira mwa Yesu, ife tikudziwa kuti uthenga wabwino wa chitetezero ndi ubatizo ndi mwazi wa Yesu. Pamene ife takhulupilira mwa Yesu, ife tiyenera kumvetsetsa uthenga wabwino wa chitetezero kudzera m’mau Wake ndi kudziwa makamaka momwe Iye anatsukira machimo athu onse.
Tiyeneranso kudziwa chimene chimaimiriridwa ndi thonje lamadzi, lofiirira, ndi lofiira pa chipata cha chihema chopatulika. Ndipo, tikhoza kukhala ndi chikhulupiriro choona chimene chidzakhala mpaka muyaya.
 
 
Ife Sitingabadwe konse Mwatsopano popanda Kukhulupilira mwa Yesu, amene ali chikoka chenicheni cha Thonje la Lamadzi, Lofiirira, ndi Lofiira
 
Kodi ansembe ankachita chiyani iwo asanalowe m’malo opatulika?
Iwo ankasambitsa manja ao ndi mapazi mu mkhate wa mkuwa.
 
Ambuye wathu anatipulumutsa ife. Ife sitingadzithandize koma kutamanda Ambuye pamene ife taona momwe Iye anatipulumutsira ife mwangwiro. Ife tiyenera kuyang’ana pa chihema chopatulika. Iye anatipatsa ife mau a uthenga wabwino wa chitetezero kudzera mu thonje lamadzi, lofiirira, ndi lofiira la chihema chopatulika ndipo anatipulumutsa ife ndi iwo. Ife tikuyamika ndi kutamanda Ambuye.
Ochimwa sankalowa m’malo opatulika. Kodi winawake amene ali ndi uchimo akanalowa bwanji m’malo opatulika? Izi zikanakhala zosatheka. Ngati munthu ameneyo walowa, iye akanaphedwa nthawi yomweyo. Ilo silikanakhala dalitso, koma tembelero. Wochimwa sankalowa m’malo opatulika ngakhalenso kuyembekeza kukhala ndi moyo.
Ambuye wathu anatipulumutsa ife kudzera mu chinsinsi chobisika mu chipata ku chihema chopatulika. Ndi thonje lamadzi, lofiirira, ndi lofiira, ndi ulusi wa bafuta, Iye anatipulumutsa ife. Ndipo Iye anatiuza ife chinsinsi cha chipulumutso Chake kudzera mu zinthu zimenezi.
Kodi inu ndi ine tinapulumutsidwa mwanjira yotero? Ngati sitikukhulupirira mau a thonje lamadzi, lofiirira, ndi lofiira, sipangakhale chipulumutso kudzera mu uthenga wabwino wa chitetezero. Mtundu wamadzi sutanthauza God, uwo umatanthauza ubatizo wa Yesu. Uwo umatanthauza ubatizo wa Yesu amene anatenga machimo athu onse.
Munthu angathe kulowa kufikira pa guwa la nsembe yopsereza popanda kukhulupirira mu thonje lamadzi. Komabe, iye sangalowe m’malo opatulika momwe God amakhala.
Choncho, tisanalowe pa chipata cha chihema chopatulika, tiyenera kukhulupirira mu thonje lamadzi (ubatizo wa Yesu), thonje lofiira (mwazi Wake pa mtanda), ndi thonje lofiirira (Yesu pokhala God ndi Mwana wa God). Pokhapo pamene ife takhulupirira ndi pamene ife timavomerezedwa ndi God ndi kulolezedwa kulowa kudzera mu chinsaru chotchinga cha Malo Opatulika Kwambiri.
Ena amalowa kunja kwa bwalo la chihema ndi kuganiza ngati kuti iwo ali mkati. Koma ichi ichi sichipulumutso. Kodi ife tiyenera kupita motalika bwanji kuti tipulumutsidwe? Ife tiyenera kukhala otha kulowa m’Malo Opatulika Kwambiri.
Kuti tilowe m’Malo opatulika kwambiri, ife tiyenera kudutsa mkhate wa mkuwa. Mkhate wa mkuwa umaimira ubatizo wa Yesu, ndipo ife tiyenera kutsuka machimo athu onse a tsiku ndi tsiku ndi ubatizo wa Yesu ndi kukhala oyeretsedwa kuti tilowe m’malo opatulika.
M’chipangano Chakale, ansembe ankayenera kuzisambitsa okha iwo asanalowe, ndipo m’Chipangano Chatsopano, Yesu anasambitsa mapazi a ophunzira Wake kuti atanthauze kutsuka kwa zolakwa za moyo wao wonse.
Lamulo la God limanena kuti, “Pakuti mphotho yake ya uchimo ndi imfa; koma mphatso yaulere ya Mulungu(God) ndiyo moyo wosatha wa mwa Khristu Yesu Ambuye wathu.” (Aroma 6:23) God amaweruza machimo a munthu popanda kuchotsera, koma Iye anawapereka kwa Mwana Wake ndi kumuweruza Iye m’malo mwake. Ichi ndi chikondi cha God, chipulumutso Chake. Chipulumutso choona chimapezeka pokhapo pamene ife takhulupirira mu uthenga wabwino wa chitetezero, ubatizo, mwazi, imfa, ndi kuuka kwa Yesu.
 
 
Kuti Abadwe Mwatsopano, Wina Sayenera konse Kunyoza Mau Olembedwa a God, Uthenga Wabwino wa Chitetezero cha Machimo
 
Kodi ndi chinthu chiti chokha chimene chatsala kwa ife kuchita?
Ndi kukhulupilira m’mau olembedwa a God. 
 
Ine sindinyoza konse anthu ena. Pamene winawake akulankhula za chinachake chimene sindikuchidziwa, ndimawapempha iwo kuti andiphunzitse ine. Koma pamene ndidafunsa za tanthauzo la chihema chopatulika, palibe amene ankandiuza ine.
Ndiye kodi ndikanachita chiyani? Ndidayenera kubwerera m’Baibulo. Mu Baibulo, kodi chihema chopatulika chafokozedwa pati? Icho chafotokozedwa mwatsanetsatane mu Eksodo. Ndipo ngati wina wawerenga buku limeneli mosamala, iye angamvetsetse tanthauzo lake kudzera m’mau olembedwa a God.
Okondendwa anzanga, inu simungapulumutsidwe pokhulupilira mwa Yesu mwakhungu. Inu simungabadwe mwatsopano chifukwa chongopita ku mpingo kawirikawiri. Ife tikudziwa zimene Yesu anauza Nikodemo. “Indetu, indetu, ndinena ndi iwe, Ngati munthu sabadwa mwa madzi ndi Mzimu Woyera, sangathe kulowa ufumu wa Mulungu(God)... Kodi uli mphunzitsi wa Israele, ndipo sudziwa izi?” (Yohane 3:5, 10) 
Onse amene akhulupirira mwa Yesu ayenera kukhulupirira mu thonje lamadzi (machimo onse a dziko anaperekedwa kwa Yesu pamene Iye anabatizidwa), thonje lofiira (imfa ya Yesu chifukwa cha machimo athu onse), ndi thonje lofiirira (Yesu ndi Mpulumutsi, God, ndi Mwana wa God).
Ife tiyenera kukhulupilira kuti Yesu Mpulumutsi wa ochimwa onse a dziko lapansi. Popanda Chikhulupiriro chimenechi, wina sangabadwe mwatsopano konse, ngakhalenso iye sangalowe m’malo opatulika a ufumu wa God. Wina sangakhale mkomwe mokhulupirika m’dziko lino lapansi popanda icho.
Kodi sichingakhale chophweka ngati munthu angabadwe mwatsopano pongokhala ndi Chikhulupiriro mwa Yesu? ―Inde.― “♫ Inu mwapulumutsidwa. Ndapulumutsidwa. Ife tonse tapulumutsidwa.♫” Kodi ndi zabwino bwanji. Koma pali ambiri amene amakhulupilira mwa Yesu popanda ‘kubadwadi mwatsopano’.
Munthu ayenera kudziwa choonadi m’Baibulo komanso kukhala ndi Chikhulupiriro mwa Yesu. Tiyenera kudziwa uthenga wabwino wa Kutsuka machimo m’Baibulo ndi tanthauzo la thonje lamadzi, lofiirira, ndi lofiira kuti tilowe m’chihema chopatulika ndi kukhala ndi God m’dziko la chikhulupiriro. Mkati mwa chihema cha Chikhulupiriro, ife tingakhale mosangalala kufikira nthawi yopita ku ufumu wa kumwamba. Ndi kofunika kuti ife tidziwe momwe tingakhulupilire mwa Yesu mu njira yoyenera.
 
 
Uthenga Wabwino Woyambirira Umabala Chiyero ndi Thonje Lamadzi 
 
Kodi chomwe chili chofunikira kwambiri pa chipulumutso ndi chiyani? 
Ubatizo wa Yesu
 
Nthawi zina winawake amaganiza kuti iye angakhale mwangwiro popanda kulakwitsa. Komabe, pamene iye akuyesa kuchita chinachake, iye posachedwa adzaona zolakwa zake. Anthu ndi operewera, ndipo ndi zosatheka kwa iwo osachimwa. Komabe, chifukwa Yesu anatipulumutsa ife ndi thonje lamadzi, lofiirira, ndi lofiira, uthenga wabwino wa chitetezero, ife tikhoza kuyeretsedwa ndi kulowa m’malo opatulika a God.
Ngati God sanatipulumutse ife ndi thonje lamadzi, ndi lofiirira, ndi lofiira, ife sitikanatha konse kulowa m’malo opatulika mwa ife tokha. Kodi chifukwa cha chimenechi ndi chiyani? Ngati okhawo amene amakhala mwangwiro ndi thupi lao ndi amene akanalowa, ndiye kuti sipakanakhala munthu woyenerera. Pamene wina wakhulupilira mwa Yesu popanda uthenga wabwino, iye amangoonjezera kokha machimo mu mtima mwake.
Yesu anatipulumutsa ndi chipulumutso chake chokonzedwa mwatcheru, chipulumutso cha thonje lamadzi, lofiirira, ndi lofiira, ndi ulusi wa bafuta. Iye anatsuka machimo athu onse. Kodi inu mukukhulupilira mu zimenezi? ―Inde.― Kodi muli ndi choonadi mu mtima mwanu cha uthenga wabwino wa Kutsuka machimo ndi kuchitira umboni ku icho? ―Inde.―
Pokhapo pamene inu muchitira umboni za uthenga wabwino ndi pamene inu mungavale pa mphumi panu mkuzi umene umanena kuti, ‘KUPATULIKIRA YEHOVA’ ndi kukhala pamodzi ndi ‘Ansembe acifumu’ (1 Petro 2:9). Pokhapo ndi pamene inu mungaime pamaso pa anthu ndi kuuza iwo kuti ndinu mtumiki wa God, wogwira ntchito monga mkulu wansembe.
Nduwira ya mkulu wansembe ili ndi mbale ya golide ndipo mbaleyo imangidwa ndi chingwe chamadzi. Chifukwa chiyani chamadzi? Chifukwa chakuti Yesu anatipulumutsa ife ndi uthenga wabwino wa Kutsuka machimo, chifukwa chakuti Iye anatenga machimo athu onse ndi kutipanga ife kukhala opanda uchimo kudzera mu ubatizo Wake (kuika manja m’Chipangano Chakale, ubatizo m’Chipangano Chatsopano).
Ngakhale tikakhulupirira mwa Yesu mwakhama chotani, sitikanatha kupeza mbale yosema ‘KUPATULIKIRA YEHOVA’ popanda mau achinsinsi a thonje lamadzi, lofiirira, ndi lofiira.
Kodi ife tinakhala bwanji olungama? Kwalembedwa mu Mateyu 3:15 kuti, “Pakuti kuyenera ife kukwaniritsa chilungamo chonse motero.” Yesu anabatizidwa ndi kutipulumutsa ife ku machimo onse a dziko lapansi. Chifukwa Iye anabatizidwa ndi kuchotsa machimo athu onse, ife okhulupirira takhala olungama.
Kodi ife tikananena bwanji kuti ife tinalibe uchimo ngati kukanakhala kuti kudalibe ubatizo wa Yesu? Ngakhale ife tinakhulupilira mwa Yesu, ngakhale ife tinalira, poganizira kupachikidwa kwa Yesu, misozi yonse m’dziko lino lapansi sikanatsuka machimo anthu onse. Ayi. Ngakhale ife tikanalira mochuruka bwanji ndi kulapa, machimo athu akanatsalirabe mkati mwa ife.
‘KUPATULIKIRA YEHOVA’. Chifukwa Iye anachotsa machimo athu onse ndi ubatizo Wake ndi mwazi Wake, chifukwa God analola machimo onse a ife ochimwa kuperekedwa kwa Yesu, chifukwa mau a chipulumutso alembedwa m’Baibulo, ife takhala olungama kudzera mu chikhulupiriro chathu ngakhale zoperewera zathu zonse.
Choncho, ife tsopano tingaime pamaso pa God. Ife tsopano tingakhale monga olungama ndi kulalikira uthenga wabwino ku dziko lapansi. “♪Oh, ndapulumutsudwa. Inu mwapulumutsidwa. Ife tonse tapulumutsidwa.♪” Ife tapulumutsidwa malingana ndi chikonzero cha God.
Popanda mau a uthenga wabwino wa chitetezero mu mtima mwanu, mulibe chipulumutso, ngakhale inu mungayese bwanji. Zili ngati nyimbo yodziwika kwambiri yokhudza chikondi cha mbali imodzi. “♫Oh, mtima wanga umagunda mwachangu popanda chifukwa nthawi zonse pamene ndaona iye, nthawi zonse pamene ndamuyandikira iye. Ndiyenera kuti ndili mu chikondi.♫” Mtima wanga umagunda mwachangu, koma osati wake. Mwatsoka, chikondi changa konse sichibwezeredwa.
Anthu amakonda kuganiza kuti chipulumutso chimabwera m’njira zambiri zosiyana kwa anthu ambiri osiyana. Iwo amafunsa kuti, “Kodi ndi chifukwa chiyani icho chiyenera kubwera podzera kokha mu uthenga wabwino wa ubatizo?” Ngati icho sichibwera kudzera mu uthenga wabwino wa ubatizo wa Yesu, ndiye kuti icho si chipulumutso chathunthu. Ndi njira yokha imene tingakhale olungama pamaso pa God chifukwa ndi njira yokha imene tingayeretsedwe kwathunthu ku machimo athu onse.
 
 
Kodi Ndi Chiyani Chipulumutso cha Thonje Lamadzi Chimene Yesu Anatipatsa Ife?
 
Kodi ndi chiyani chimene chatipanga ife kukhala olungama?
Uthenga wabwino wa thonje lamadzi, lofiirira, ndi lofiira
 
Chipulumutso kudzera mu uthenga wabwino wa thonje lamadzi, lofiirira, ndi lofiira ndi mphatso ya God kwa anthu onse. Mphatso iyi yatilola ife kulowa m’chihema chopatulika ndi kukhala mu mtendere. Yatipanga ife kukhala olungama. Yatipanga ife kukhala olungama ndi kutilola kukhala mkati mwa mpingo kuti tiphunzitsidwe mau opatulika mkati mwa mpingo.
Nthawi zonse pamene ife tapita pamaso pa God kukapemphera, uthenga wabwino umatidalitsa ife ndi chikondi Wake. Ichi ndi chifukwa chake chipulumutso ndi cha mtengo wapatali kwa ife. Yesu akutiuza ife kuti timange nyumba ‘pa thanthwe’. Thanthwe ndi ubatizo wa Yesu. Ife tonse tidzapulumutsidwa, kukhala mu chisomo ngati ana a God, ndipo kenaka kupita kumwamba kukhala moyo wosatha.
Okondedwa anzanga, chifukwa cha uthenga wabwino wa chitetezero, ndife othekera kulowa mu chihema chopatulika ndi Chikhulupiriro. Chifukwa cha kutsuka kwa machimo athu onse (Ubatizo wa Yesu) ndi chiweruzo pa mtanda, ife tapulumutsidwa pokhala ndi Chikhulupiriro. 
Chitetezero chochuluka cha machimo athu onse, ubatizo ndi mwazi wa Yesu, ndi uthenga wabwino umene unatsuka machimo athu onse. Kodi inu mukukhulupilira zimenezi? Uthenga wabwino woona ndi uthenga wabwino wa kumwamba wa chitetezero umene watsuka motheratu machimo athu onse.
Ife tabadwa mwatsopano pokhulupilira mu uthenga wabwino wa chitetezero. Yesu watipatsa ife uthenga wabwino wa chitetezero, umene watsuka machimo athu onse a tsiku ndi tsiku komanso ngakhale machimo onse a m’tsogolo. Tikutamanda Ambuye. Aleluya! Zikomo kwa Ambuye.
Uthenga wabwino wa madzi ndi Mzimu Woyera (Uthenga Wabwino wa madzi ndi mwazi) ndi uthenga wabwino woona olankhulidwa ndi Yesu Kristu. Buku limeneli linalembedwa kuti livumbulutse uthenga wabwino wa Yesu, uthenga wabwino wa madzi ndi Mzimu Woyera.
Chifukwa anthu ambiri amakhulupirira mwa Yesu popanda kudziwa choonadi chathunthu, tsopano akugwira ntchito kokha m’dziko la zaumulungu za Chikristu (zotchedwa zaumulungu za filosofi); mwachidule, amakhala mu chiphunzitso cholakwika ndi chisokonezo. Choncho, tiyenera kubwerera ndi kukhulupirira mu uthenga wabwino woona. Sikunachedwe kwambiri.
Ndikufuna ndifotokoze mwatsatanetsatane kwambiri m’buku lachiwiri kwa iwo amene ali ndi mafunso okhudza za uthenga wabwino wa kubadwa mwatsopano mwa madzi ndi Mzimu Woyera.
 
Ulaliki uwu ukupezekanso mu mtundu wa ebook. Dinani pachikuto cha buku pansipa.
KODI MWABADWADI MWATSOPANO MWA MADZI NDI MZIMU WOYERA? [Kusindikiza Kokonzedwanso Kwatsopano]